Masalimo 20 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 20:1-9

Salimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.

2Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;

akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.

3Iye akumbukire nsembe zako zonse

ndipo alandire nsembe zako zopsereza.

Sela

4Akupatse chokhumba cha mtima wako

ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.

5Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana

ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,

Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

6Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;

Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika

ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.

7Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo

koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.

8Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,

koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

9Inu Yehova, pulumutsani mfumu!

Tiyankheni pamene tikuyitanani!

New Russian Translation

Псалтирь 20:1-14

Псалом 20

1Дирижеру хора. Псалом Давида.

2Господи, царь радуется силе Твоей,

о победах20:2 Или: «спасении». Твоих радуется безмерно.

3Ты исполнил то, чего он желал,

и мольбы его не отверг. Пауза

4Ты встретил его с обильными благословениями,

возложил на голову его венец из чистого золота.

5Он просил жизни, и Ты дал ему

долгоденствие навеки.

6Велика его слава из-за побед, что Ты даровал;

Ты возложил на него честь и величие.

7Ты одарил его вечными благословениями

и исполнил радости от Твоего присутствия.

8Ведь царь надеется на Господа,

и по милости Всевышнего не поколеблется.

9Твоя рука схватит врагов Твоих,

правая рука Твоя – ненавистников Твоих.

10Во время явления Твоего

Ты сделаешь их подобными горящей печи.

В гневе Своем Господь их погубит,

и огонь Его их сожжет.

11Ты истребишь с земли их детей,

из людской среды их потомство.

12Они против Тебя замышляют зло

и строят козни, но безуспешно.

13Ты в бегство их обратишь,

нацелив в них натянутый лук.

14В силе Твоей вознесись, Господи!

Мы Твою мощь воспоем и прославим.