Masalimo 20 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 20:1-9

Salimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.

2Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;

akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.

3Iye akumbukire nsembe zako zonse

ndipo alandire nsembe zako zopsereza.

Sela

4Akupatse chokhumba cha mtima wako

ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.

5Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana

ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,

Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

6Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;

Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika

ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.

7Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo

koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.

8Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,

koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

9Inu Yehova, pulumutsani mfumu!

Tiyankheni pamene tikuyitanani!

New International Reader’s Version

Psalm 20:1-9

Psalm 20

For the director of music. A psalm of David.

1May the Lord answer you when you are in trouble.

May the God of Jacob keep you safe.

2May he send you help from the sacred tent.

May he give you aid from Zion.

3May he remember all your sacrifices.

May he accept your burnt offerings.

4May he give you what your heart wishes for.

May he make all your plans succeed.

5May we shout for joy over your victory.

May we lift up our flags in the name of our God.

May the Lord give you everything you ask for.

6Now I know that the Lord gives victory to his anointed king.

He answers him from his sacred home in heaven.

The power of God’s right hand gives victory to the king.

7Some trust in chariots. Some trust in horses.

But we trust in the Lord our God.

8They are brought to their knees and fall down.

But we get up and stand firm.

9Lord, give victory to the king!

Answer us when we call out to you!