Masalimo 20 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 20:1-9

Salimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.

2Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;

akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.

3Iye akumbukire nsembe zako zonse

ndipo alandire nsembe zako zopsereza.

Sela

4Akupatse chokhumba cha mtima wako

ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.

5Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana

ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,

Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

6Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;

Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika

ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.

7Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo

koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.

8Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,

koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

9Inu Yehova, pulumutsani mfumu!

Tiyankheni pamene tikuyitanani!

La Bible du Semeur

Psaumes 20:1-10

Fais triompher notre Roi !

1Au chef de chœur. Cantique de David.

2Que l’Eternel t’exauce ╵au jour de la détresse,

et que le Dieu de Jacob te protège.

3Que, de son sanctuaire, ╵il t’envoie du secours,

et que, depuis Sion, ╵il te soutienne !

4Qu’il tienne compte ╵de toutes tes offrandes,

et que tes holocaustes ╵soient agréés par lui.

Pause

5Qu’il daigne t’accorder ╵ce que ton cœur souhaite !

Qu’il fasse s’accomplir ╵tout ce que tu projettes !

6Pour fêter ta victoire, ╵nous crierons notre joie,

déployant nos bannières ╵pour la gloire de notre Dieu.

Que l’Eternel ╵exauce toutes tes requêtes !

7Oui, je sais maintenant, ╵que l’Eternel sauve son roi ╵qui a reçu l’onction,

il lui répond ╵de sa demeure sainte au ciel,

en opérant sa délivrance ╵par l’action de sa force.

8Aux uns, les chars de guerre, ╵aux autres, les chevaux.

Pour notre part, ╵c’est sur l’Eternel, notre Dieu ╵que nous comptons.

9Eux, ils fléchissent et ils tombent,

nous, nous restons debout ╵et tenons fermement.

10Eternel, sauve notre roi !

Qu’il nous réponde ╵quand nous faisons appel à lui20.10 Qu’il nous réponde: l’ancienne version grecque a : Réponds-nous. Il faut alors traduire la suite : quand nous faisons appel à toi..