Salimo 2
1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?
Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;
ndipo olamulira asonkhana pamodzi
kulimbana ndi Ambuye
ndi wodzozedwa wakeyo.
3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo
ndipo titaye zingwe zawo.”
4Wokhala mmwamba akuseka;
Ambuye akuwanyoza iwowo.
5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake
ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga
pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:
Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;
lero Ine ndakhala Atate ako.
8Tandipempha,
ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;
malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;
udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10Kotero, inu mafumu, chenjerani;
chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11Tumikirani Yehova mwa mantha
ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;
kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,
pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.
Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.
Salmo 2
1¿Por qué se rebelan2:1 se rebelan. Alt. se enfurecen (LXX). las naciones
y en vano conspiran los pueblos?
2Los reyes de la tierra se rebelan;
los gobernantes se confabulan contra el Señor
y contra su ungido.
3Y dicen: «¡Hagamos pedazos sus cadenas!
¡Librémonos de su yugo!».
4El que está en el trono de los cielos se ríe;
el Señor se burla de ellos.
5En su enojo los reprende,
en su furor los asusta y dice:
6«He establecido a mi rey
sobre Sión, mi santo monte».
7Yo proclamaré el decreto del Señor:
«Tú eres mi hijo», me ha dicho,
«hoy mismo te he engendrado.
8Pídeme,
y como herencia te entregaré las naciones;
serán tu propiedad los confines de la tierra.
9Las gobernarás con cetro de hierro;
las harás pedazos como a vasijas de barro».
10Por eso ustedes, los reyes, sean prudentes;
déjense enseñar, gobernantes de la tierra.
11Sirvan al Señor con temor;
con temblor ríndanle alabanza.
12Besen al hijo,2:12 Besen al hijo. Texto de difícil traducción. no sea que se enoje
y sean ustedes destruidos en el camino,
pues su ira se inflama de repente.
¡Dichosos los que en él buscan refugio!