Masalimo 2 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 2:1-12

Salimo 2

1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?

Akonzekeranji zopanda pake anthu?

2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.

3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo

ndipo titaye zingwe zawo.”

4Wokhala mmwamba akuseka;

Ambuye akuwanyoza iwowo.

5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake

ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,

6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga

pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;

lero Ine ndakhala Atate ako.

8Tandipempha,

ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;

malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.

9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;

udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10Kotero, inu mafumu, chenjerani;

chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.

11Tumikirani Yehova mwa mantha

ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.

12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;

kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,

pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.

Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

Nueva Versión Internacional

Salmo 2:1-12

Salmo 2

1¿Por qué se rebelan2:1 se rebelan. Alt. se enfurecen (LXX). las naciones

y en vano conspiran los pueblos?

2Los reyes de la tierra se rebelan;

los gobernantes se confabulan contra el Señor

y contra su ungido.

3Y dicen: «¡Hagamos pedazos sus cadenas!

¡Librémonos de su yugo!».

4El que está en el trono de los cielos se ríe;

el Señor se burla de ellos.

5En su enojo los reprende,

en su furor los asusta y dice:

6«He establecido a mi rey

sobre Sión, mi santo monte».

7Yo proclamaré el decreto del Señor:

«Tú eres mi hijo», me ha dicho,

«hoy mismo te he engendrado.

8Pídeme,

y como herencia te entregaré las naciones;

serán tu propiedad los confines de la tierra.

9Las gobernarás con cetro de hierro;

las harás pedazos como a vasijas de barro».

10Por eso ustedes, los reyes, sean prudentes;

déjense enseñar, gobernantes de la tierra.

11Sirvan al Señor con temor;

con temblor ríndanle alabanza.

12Besen al hijo,2:12 Besen al hijo. Texto de difícil traducción. no sea que se enoje

y sean ustedes destruidos en el camino,

pues su ira se inflama de repente.

¡Dichosos los que en él buscan refugio!