Masalimo 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 2:1-12

Salimo 2

1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?

Akonzekeranji zopanda pake anthu?

2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.

3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo

ndipo titaye zingwe zawo.”

4Wokhala mmwamba akuseka;

Ambuye akuwanyoza iwowo.

5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake

ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,

6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga

pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;

lero Ine ndakhala Atate ako.

8Tandipempha,

ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;

malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.

9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;

udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10Kotero, inu mafumu, chenjerani;

chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.

11Tumikirani Yehova mwa mantha

ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.

12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;

kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,

pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.

Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

New International Reader’s Version

Psalm 2:1-12

Psalm 2

1Why do the nations plan evil together?

Why do they make useless plans?

2The kings of the earth rise up against the Lord.

The rulers of the earth join together against his anointed king.

3“Let us break free from their chains,” they say.

“Let us throw off their ropes.”

4The God who sits on his throne in heaven laughs.

The Lord makes fun of those rulers and their plans.

5When he is angry, he warns them.

When his anger blazes out, he terrifies them.

6He says to them,

“I have placed my king on my holy mountain of Zion.”

7I will announce what the Lord has promised.

He said to me, “You are my son.

Today I have become your father.

8Ask me, and I will give the nations to you.

All nations on earth will belong to you.

9You will break them with an iron scepter.

You will smash them to pieces like clay pots.”

10Kings, be wise!

Rulers of the earth, be warned!

11Serve the Lord and have respect for him.

Celebrate his rule with trembling.

12Obey the son completely, or he will be angry.

Your way of life will lead to your death.

His anger can blaze out at any moment.

Blessed are all those who go to him for safety.