Masalimo 19 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 19:1-14

Salimo 19

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;

thambo limalalikira ntchito za manja ake.

2Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,

usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.

3Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;

liwu lawo silimveka.

4Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,

mawuwo amafika mpaka

kumalekezero a dziko lapansi.

5Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,

ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.

6Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo

ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;

palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.

7Lamulo la Yehova ndi langwiro,

kutsitsimutsa moyo.

Maumboni a Yehova ndi odalirika,

amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.

8Malangizo a Yehova ndi olungama,

amapereka chimwemwe mu mtima.

Malamulo a Yehova ndi onyezimira,

amapereka kuwala.

9Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,

chimakhala mpaka muyaya.

Maweruzo a Yehova ndi owona

ndipo onse ndi olungama;

10ndi a mtengowapatali kuposa golide,

kuposa golide weniweni;

ndi otsekemera kuposa uchi,

kuposa uchi wochokera pa chisa chake.

11Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;

powasunga pali mphotho yayikulu.

12Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?

Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.

13Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;

iwo asandilamulire.

Kotero ndidzakhala wosalakwa,

wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

14Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

Nueva Versión Internacional

Salmo 19:1-14

Salmo 19Sal 19 En el texto hebreo 19:1-14 se numera 19:2-15.

Al director musical. Salmo de David.

1Los cielos cuentan la gloria de Dios;

la expansión proclama la obra de sus manos.

2Un día transmite el mensaje al otro día;

una noche a la otra comparte sabiduría.

3Sin palabras, sin lenguaje,

sin una voz perceptible,

4por toda la tierra resuena su eco;

sus palabras llegan hasta los confines del mundo.

Dios ha establecido en los cielos

un hogar para el sol.

5Y este, como novio que sale de la cámara nupcial,

se regocija, cual poderoso guerrero, al recorrer su camino.

6Sale de un extremo de los cielos

y, en su recorrido, llega al otro extremo,

sin que nada se libre de su calor.

7La Ley del Señor es perfecta:

infunde nuevo aliento.

El mandato del Señor es digno de confianza:

da sabiduría al sencillo.

8Los preceptos del Señor son rectos:

traen alegría al corazón.

El mandamiento del Señor es claro:

da luz a los ojos.

9El temor del Señor es puro:

permanece para siempre.

Las ordenanzas del Señor son verdaderas:

todas ellas son justas.

10Son más deseables que el oro,

más que mucho oro refinado;

son más dulces que la miel,

la miel que destila del panal.

11Por ellas queda advertido tu siervo;

quien las obedece recibe una gran recompensa.

12¿Quién está consciente de sus propios errores?

¡Perdóname aquellos de los que no estoy consciente!

13Libra, además, a tu siervo de pecar a sabiendas;

no permitas que tales pecados me dominen.

Entonces seré íntegro,

inocente de un gran pecado.

14Sean, pues, aceptables ante ti

mis palabras y mis meditaciones

oh Señor, mi roca y mi redentor.