Masalimo 19 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 19:1-14

Salimo 19

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;

thambo limalalikira ntchito za manja ake.

2Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,

usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.

3Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;

liwu lawo silimveka.

4Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,

mawuwo amafika mpaka

kumalekezero a dziko lapansi.

5Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,

ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.

6Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo

ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;

palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.

7Lamulo la Yehova ndi langwiro,

kutsitsimutsa moyo.

Maumboni a Yehova ndi odalirika,

amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.

8Malangizo a Yehova ndi olungama,

amapereka chimwemwe mu mtima.

Malamulo a Yehova ndi onyezimira,

amapereka kuwala.

9Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,

chimakhala mpaka muyaya.

Maweruzo a Yehova ndi owona

ndipo onse ndi olungama;

10ndi a mtengowapatali kuposa golide,

kuposa golide weniweni;

ndi otsekemera kuposa uchi,

kuposa uchi wochokera pa chisa chake.

11Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;

powasunga pali mphotho yayikulu.

12Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?

Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.

13Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;

iwo asandilamulire.

Kotero ndidzakhala wosalakwa,

wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

14Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

New Russian Translation

Псалтирь 19:1-10

Псалом 19

1Дирижеру хора. Псалом Давида.

2Да ответит Господь тебе в день печали.

Да хранит тебя имя Бога Иакова.

3Да пошлет Он помощь тебе из святилища

и поддержит тебя с Сиона.

4Да вспомнит Он все жертвы твои

и всесожжения твои примет. Пауза

5Да даст Он тебе то, чего ты желаешь,

и исполнит все твои намерения.

6Мы будем кричать от радости о твоей победе

и поднимем знамена во имя нашего Бога.

Да исполнит Господь все твои просьбы.

7Теперь я знаю: Господь спасает Своего помазанника,

отвечает ему со святых небес Своих

спасающей силой Своей правой руки.

8Кто хвалится колесницами, а кто конями,

мы же хвалимся именем Господа, нашего Бога.

9Они ослабели и падают,

а мы поднимаемся и стоим твердо.

10Господи, даруй царю победу!

Ответь нам19:10 Или: «даруй победу; царь, ответь нам»., когда мы взываем!