Masalimo 18 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 18:1-50

Salimo 18

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.

1Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

2Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo.

Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.

3Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

4Zingwe za imfa zinandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

5Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

6Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize.

Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.

7Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

ndipo maziko a mapiri anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

8Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

9Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

10Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

11Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.

12Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,

makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.

13Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

14Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

15Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;

maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.

16Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

17Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.

18Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

19Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

20Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

21Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.

22Malamulo ake onse ali pamaso panga;

sindinasiye malangizo ake.

23Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

24Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.

25Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

26kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

27Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.

28Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;

Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

29Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

30Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa Iye.

31Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

32Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

33Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

34Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

35Inu mumandipatsa chishango chachipambano,

ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza;

mumawerama pansi kundikuza.

36Munakulitsa njira yoyendamo ine,

kuti mapazi anga asaguluke.

37Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;

sindinabwerere mpaka atawonongedwa.

38Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;

anagwera pa mapazi anga.

39Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,

munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.

40Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,

ndipo ine ndinawononga adani angawo.

41Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.

42Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.

Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

43Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;

mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

44Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine amandigonjera.

45Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

46Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!

Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!

47Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,

48amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

49Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

50Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;

amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

O Livro

Salmos 18:1-50

Salmo 18

(2 Sm 22.1-51)

Este cântico de David foi dirigido ao Senhor quando o libertou dos seus inimigos, incluindo Saul.

1Eu te amo, Senhor, tu que és a minha força.

2O Senhor é o meu rochedo,

o meu lugar forte e o meu libertador.

Esconder-me-ei em Deus

que é a minha rocha e o meu alto retiro.

Ele é o meu escudo,

o poder da minha salvação e o meu refúgio.

3Invocarei o Senhor que é digno de todo o louvor;

salvar-me-á de todos os meus adversários.

4Cercaram-me laços de morte;

torrentes de maldade desabaram sobre mim.

5Fui ligado e atado por laços do mundo dos mortos e por ciladas da morte.

6Clamei pelo Senhor, meu Deus, na minha tribulação,

e ele ouviu-me desde o seu templo;

o meu clamor chegou aos seus ouvidos.

7Então a Terra foi abalada e tremeu;

os fundamentos das montanhas abalaram-se,

por causa da sua ira.

8Saiu fumo do seu rosto,

da sua boca um fogo devorador que tudo consumia,

e punha as brasas a arder.

9Fez baixar os céus e desceu,

andando sobre espessas nuvens.

10Voou sobre um querubim,

sobre as asas do vento.

11As trevas rodearam-no,

espessas nuvens o circundaram.

12O brilho da sua presença resplandeceu,

com nuvens, relâmpagos e tempestades de granizo.

13O Senhor trovejou desde os céus;

o Deus supremo fez ecoar a sua voz.

14Disparou as suas frechas de luz

e dispersou os inimigos.

15Pelo sopro da tua respiração,

até o mar se dividiu em dois;

viu-se o fundo das águas

pela repreensão do Senhor.

16Desde o alto me livrou,

salvou-me de ser levado pelas vagas.

17Libertou-me do meu poderoso inimigo,

daqueles que me odiavam,

dos que tinham muito mais força do que eu.

18Saltaram sobre mim, no dia da calamidade,

mas o Senhor foi a minha proteção.

19Fez-me reaver a liberdade;

resgatou-me, porque me amava.

20O Senhor recompensou-me,

conforme a minha retidão,

porque tinha as mãos limpas.

21Guardei os caminhos do Senhor;

não me afastei impiamente do meu Deus.

22Tive sempre presentes as suas leis;

não me desviei dos seus estatutos.

23Fui sempre reto perante ele

e fugi do pecado.

24Por isso, o Senhor atendeu à minha justiça,

pois viu que eu estava limpo.

25Tu és misericordioso para com os misericordiosos;

revelas a tua retidão para com os que são retos.

26Com os puros, mostras-te puro,

mas astuto com os perversos.

27Salvas os que estão aflitos, mas abates os orgulhosos,

mas humilhas os que têm olhar altivo.

28Senhor, meu Deus, tu acendes a minha luz!

Transformas em luz a minha escuridão.

29Pelo teu poder posso esmagar um exército;

pela tua força saltarei muralhas.

30O caminho de Deus é reto.

A palavra do Senhor é verdade;

é um escudo para os que procuram a sua proteção.

31Só o Senhor é Deus.

Quem é como um rochedo senão o nosso Deus?

32Deus é quem me fortalece;

faz-me andar em perfeita segurança.

33Faz com que caminhe com passo bem firme,

como as gazelas sobre os cumes.

34Torna-me hábil nos combates,

dá-me força capaz de dobrar um arco de bronze;

35Deste-me o escudo da tua salvação;

amparaste-me com a tua mão direita

e com a tua bondade me engrandeceste.

36Fizeste-me andar sobre caminhos planos,

onde os meus pés não vacilaram.

37Persegui os meus inimigos e os alcancei;

não desisti sem os derrotar.

38Persegui-os e destrocei-os,

nenhum deles se poderá levantar.

Caíram debaixo dos meus pés.

39Pois deste-me força para a batalha.

Fizeste com que subjugasse

todos os que se levantaram contra mim.

40Obrigaste os meus inimigos a retroceder e fugir;

destruí todos os que me odiavam.

41Pediram ajuda, mas ninguém os auxiliou;

clamaram ao Senhor, mas recusou ouvi-los.

42Pisei-os como o pó do chão que se vai com o vento;

esmaguei-os e dispersei-os como pó nas ruas.

43Guardaste-me da rebelião do meu povo;

designaste-me para que seja cabeça das nações.

Estrangeiros me servirão.

44Em breve me serão sujeitos,

quando ouvirem falar do meu poder.

45Perderão a altivez e virão a tremer,

lá dos seus esconderijos.

46O Senhor vive!

Bendito seja aquele que é a minha rocha!

Que seja louvado o Deus da minha salvação!

47Ele é o Deus que por mim faz vingança,

que destrói os que se levantam contra mim.

48Resgataste-me dos meus adversários.

Sim, tu levantaste-me em segurança,

acima das suas cabeças.

Livraste-me da violência.

49Por isso, Senhor, dar-te-ei graças entre as nações,

e cantarei louvores ao teu nome.

50Ele deu uma maravilhosa salvação ao seu rei;

manifestou misericórdia ao seu ungido,

a David e à sua família, para sempre.