Masalimo 18 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 18:1-50

Salimo 18

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.

1Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

2Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo.

Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.

3Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

4Zingwe za imfa zinandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

5Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

6Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize.

Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.

7Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

ndipo maziko a mapiri anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

8Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

9Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

10Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

11Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.

12Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,

makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.

13Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

14Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

15Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;

maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.

16Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

17Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.

18Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

19Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

20Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

21Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.

22Malamulo ake onse ali pamaso panga;

sindinasiye malangizo ake.

23Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

24Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.

25Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

26kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

27Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.

28Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;

Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

29Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

30Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa Iye.

31Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

32Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

33Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

34Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

35Inu mumandipatsa chishango chachipambano,

ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza;

mumawerama pansi kundikuza.

36Munakulitsa njira yoyendamo ine,

kuti mapazi anga asaguluke.

37Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;

sindinabwerere mpaka atawonongedwa.

38Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;

anagwera pa mapazi anga.

39Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,

munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.

40Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,

ndipo ine ndinawononga adani angawo.

41Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.

42Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.

Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

43Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;

mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

44Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine amandigonjera.

45Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

46Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!

Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!

47Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,

48amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

49Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

50Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;

amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

Nueva Versión Internacional

Salmo 18:1-50

Salmo 18Sal 18 En el texto hebreo 18:1-50 se numera 18:2-51. Este canto de David se repite con poca variación en 2S 22:1-51.

Al director musical. De David, siervo del Señor. David dedicó al Señor la letra de esta canción cuando el Señor lo libró de las manos de todos sus enemigos y de las manos de Saúl. Dijo así:

1¡Cuánto te amo, Señor, fuerza mía!

2El Señor es mi roca, mi amparo, mi libertador;

es mi Dios, la roca en que me refugio.

Es mi escudo, el poder que me salva,18:2 el poder que me salva. Lit. el cuerno de mi salvación.

¡mi más alto escondite!

3Invoco al Señor, que es digno de alabanza,

y quedo a salvo de mis enemigos.

4Los lazos de la muerte me envolvieron;

los torrentes destructores me abrumaron.

5Los lazos del sepulcro18:5 del sepulcro. Lit. del Seol. me enredaron;

las redes de la muerte me atraparon.

6En mi angustia invoqué al Señor;

clamé a mi Dios por ayuda.

Él me escuchó desde su Templo;

¡mi clamor llegó a sus oídos!

7La tierra tembló, se estremeció;

se sacudieron los cimientos de los montes;

temblaron a causa de su enojo.

8Por la nariz echaba humo,

por la boca, fuego consumidor;

¡lanzaba carbones encendidos!

9Rasgando el cielo, descendió,

pisando sobre oscuros nubarrones.

10Montando sobre un querubín, surcó los cielos

y se remontó sobre las alas del viento.

11De las tinieblas y los oscuros nubarrones

hizo su escondite, una tienda que lo rodeaba.

12De su radiante presencia brotaron nubes,

granizos y carbones encendidos.

13En el cielo, entre granizos y carbones encendidos,

se oyó el trueno del Señor;

resonó la voz del Altísimo.

14Lanzó sus flechas y dispersó a los enemigos;

con relámpagos los desconcertó.

15A causa de tu reprensión, oh Señor,

y por el resoplido de tu enojo,18:15 por … tu enojo. Lit. por el soplo del aliento de tu nariz.

las cuencas del mar quedaron a la vista;

al descubierto quedaron los cimientos de la tierra.

16Extendiendo su mano desde lo alto,

tomó la mía y me sacó del mar profundo.

17Me libró de mi enemigo poderoso,

de aquellos que me odiaban y eran más fuertes que yo.

18En el día de mi desgracia me salieron al encuentro,

pero mi apoyo fue el Señor.

19Me sacó a un amplio espacio;

me libró porque se agradó de mí.

20El Señor me ha pagado conforme a mi justicia;

me ha premiado conforme a la limpieza de mis manos.

21He guardado los caminos del Señor

y no he cometido el error de alejarme de mi Dios.

22Presentes tengo todas sus leyes;

no me he alejado de sus estatutos.

23He sido íntegro ante él

y me he abstenido de pecar.

24El Señor me ha recompensado conforme a mi justicia,

conforme a la limpieza de mis manos ante sus ojos.

25Tú eres fiel con quien es fiel

e íntegro con quien es íntegro;

26sincero eres con quien es sincero,

pero sagaz con el que es tramposo.

27Tú das la victoria a los humildes,

pero humillas a los altivos.

28Tú, Señor, mantienes mi lámpara encendida;

tú, Dios mío, iluminas mis tinieblas.

29Con tu apoyo me lanzaré contra un ejército;

contigo, Dios mío, podré asaltar murallas.

30El camino de Dios es perfecto;

la palabra del Señor es intachable.

Escudo es Dios a los que se refugian en él.

31Pues ¿quién es Dios sino el Señor?

¿Quién es la Roca sino nuestro Dios?

32Es él quien me arma de valor

y hace perfecto mi camino;

33da a mis pies la ligereza del venado

y me mantiene firme en las alturas;

34adiestra mis manos para la batalla

y mis brazos para tensar un arco de bronce.

35Tú me cubres con el escudo de tu salvación

y con tu diestra me sostienes;

tu ayuda me ha hecho prosperar.

36Has despejado el paso de mi camino,

para que mis tobillos no se tuerzan.

37Perseguí a mis enemigos, les di alcance

y no retrocedí hasta verlos aniquilados.

38Los aplasté. Ya no pudieron levantarse.

¡Cayeron debajo de mis pies!

39Tú me armaste de valor para el combate;

doblegaste ante mí a los rebeldes.

40Hiciste retroceder a mis enemigos

y así exterminé a los que me odiaban.

41Pedían ayuda y no hubo quien los salvara.

Al Señor clamaron,18:41 Al Señor clamaron (versiones antiguas); TM no incluye clamaron. pero no respondió.

42Los desmenucé. Parecían polvo disperso por el viento.

Los pisoteé18:42 Los pisoteé (LXX, Siríaca, Targum, mss. y 2S 22:43); Los vacié (TM). como al lodo de las calles.

43Me has librado de los conflictos con el pueblo;

me has puesto por líder de las naciones;

me sirve gente que yo no conocía.

44Apenas me oyen, me obedecen;

son extranjeros y me rinden homenaje.

45Esos extraños se descorazonan

y temblando salen de sus refugios.

46¡El Señor vive! ¡Alabada sea mi Roca!

¡Exaltado sea el Dios de mi salvación!

47Él es el Dios que me vindica,

el que pone los pueblos a mis pies.

48Tú me libras de mis enemigos,

me exaltas por encima de mis adversarios,

me salvas de los hombres violentos.

49Por eso, Señor, te alabo entre las naciones

y canto salmos a tu nombre.

50Él da grandes victorias a su rey;

a su ungido David y a sus descendientes

les muestra por siempre su gran amor.