Masalimo 18 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 18:1-50

Salimo 18

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.

1Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

2Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo.

Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.

3Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

4Zingwe za imfa zinandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

5Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

6Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize.

Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.

7Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

ndipo maziko a mapiri anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

8Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

9Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

10Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

11Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.

12Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,

makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.

13Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

14Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

15Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;

maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.

16Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

17Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.

18Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

19Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

20Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

21Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.

22Malamulo ake onse ali pamaso panga;

sindinasiye malangizo ake.

23Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

24Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.

25Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

26kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

27Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.

28Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;

Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

29Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

30Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa Iye.

31Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

32Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

33Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

34Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

35Inu mumandipatsa chishango chachipambano,

ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza;

mumawerama pansi kundikuza.

36Munakulitsa njira yoyendamo ine,

kuti mapazi anga asaguluke.

37Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;

sindinabwerere mpaka atawonongedwa.

38Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;

anagwera pa mapazi anga.

39Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,

munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.

40Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,

ndipo ine ndinawononga adani angawo.

41Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.

42Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.

Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

43Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;

mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

44Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine amandigonjera.

45Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

46Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!

Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!

47Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,

48amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

49Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

50Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;

amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 18:1-50

Zabbuli 18

Ya Mukulu wa Bayimbi. Zabbuli ya Dawudi gye yayimbira Mukama bwe yamuwonya abalabe be ne Sawulo.

1Nkwagala Ayi Mukama kubanga ggwe maanyi gange.

218:2 a Zab 19:14 b Zab 59:11 c Zab 75:10Mukama lwe lwazi lwange, ky’ekigo kyange ekigumu era ye mununuzi wange,

ye Katonda wange era lwe lwazi lwange mwe neekweka;

ye ngabo yange era ye mulokozi wange ow’amaanyi, era kye kigo kyange ekinywevu.

318:3 Zab 48:1Nkoowoola Mukama asaana okutenderezebwa,

era amponya eri abalabe bange.

418:4 a Zab 116:3 b Zab 124:4Emiguwa gy’okufa gyanneetooloola;

embuyaga ez’okusaanawo zansaanikira.

518:5 Zab 116:3Ebisiba eby’amagombe byanneetooloola;

n’emitego gy’okufa ne ginjolekera.

618:6 Zab 34:15Mu nnaku yange nakoowoola Mukama;

ne nkaabirira Katonda wange annyambe.

Yawulira eddoboozi lyange ng’ali mu yeekaalu ye;

omulanga gwange ne gutuuka mu matu ge.

718:7 a Bal 5:4 b Zab 68:7-8Emisingi gy’ensi ne gikankana ne giyuuguuma;

ensozi ne zinyeenyezebwa ne ziseeseetuka,

kubanga yali asunguwadde.

818:8 Zab 50:3Omukka ne gunyooka nga guva mu nnyindo ze.

Omuliro ne guva mu kamwa ke,

ne gukoleeza amanda ne gabuubuuka.

918:9 Zab 144:5Yayabuluza eggulu n’akka wansi;

ebire ebikutte nga biri wansi w’ebigere bye.

1018:10 a Zab 80:1 b Zab 104:3Yeebagala kerubi n’abuuka,18:10 Bakerubi batonde ba Katonda era babeera mu kitiibwa kye. Be balabirira Entebe ey’Obwakabaka ey’Obwakatonda.

n’aseeyeeyeza ku biwaawaatiro by’empewo.

1118:11 Ma 4:11; Zab 97:2Yafuula ekizikiza ekyamwetooloolanga

okuba enkuufiira ey’ebire ebijjudde amazzi.

1218:12 a Zab 104:2 b Zab 97:3Okumasamasa okwali mu maaso ge ne kuva mu bire bye,

n’okumyansa kw’eggulu n’omuzira.

1318:13 Zab 29:3; 104:7Mukama yabwatuka ng’asinziira mu ggulu; oyo Ali Waggulu Ennyo yayogera;

mu kamwa ke ne muvaamu omuzira n’okumyansa kw’eggulu.

1418:14 Zab 144:6Yalasa obusaale bwe n’asaasaanya abalabe;

n’okumyansa okw’eggulu n’abawangula.

1518:15 Zab 76:6; 106:9Ebiwonvu eby’omu nnyanja ne bibikkulwa

n’emisingi gy’ensi ne gyeyerula

olw’okunenya kwo Ayi Mukama

n’olw’okubwatuka kw’omukka ogw’omu nnyindo zo.

1618:16 Zab 144:7Mukama yagolola omukono gwe ng’ali waggulu,

n’ankwata n’annyinyulula mu mazzi amangi.

1718:17 Zab 35:10Yamponya abalabe bange ab’amaanyi,

abankyawa, abo abaali bansinza amaanyi.

1818:18 Zab 59:16Bannumba nga ndi mu buzibu,

naye Mukama n’annyamba.

1918:19 a Zab 31:8 b Zab 118:5N’antwala mu kifo ekigazi n’amponya,

kubanga yansanyukira nnyo.

2018:20 Zab 24:4Mukama ankoledde ng’obutuukirivu bwange bwe buli,

ansasudde ng’ebikolwa byange ebirungi bwe biri.

2118:21 a 2By 34:33 b Zab 119:102Kubanga ntambulidde mu makubo ga Mukama,

ne sikola kibi eri Katonda wange.

2218:22 Zab 119:30Ddala ddala amateeka ga Mukama gonna ngagondedde,

era ne siva ku biragiro bye.

23Sisobyanga mu maaso ge

era nneekuuma obutayonoona.

2418:24 1Sa 26:23Noolwekyo, Mukama ansasudde ng’obutuukirivu bwange bwe buli,

era ng’ebikolwa byange ebirungi bwe biri by’alaba.

2518:25 1Bk 8:32; Zab 62:12; Mat 5:7Eri omwesigwa weeraga ng’oli mwesigwa,

n’eri atalina musango weeraga nga tolina musango.

2618:26 Nge 3:34Eri abalongoofu weeraga ng’oli mulongoofu,

n’eri abakyamu weeraga ng’obasinza amagezi.

2718:27 Nge 6:17Owonya abawombeefu,

naye abeegulumiza obakkakkanya.

2818:28 Yob 18:6; 29:3Okoleezezza ettaala yange;

Ayi Mukama Katonda wange, ekizikiza kyange okimulisizza.

2918:29 Beb 11:34Bwe mbeera naawe nsobola okulumba abalabe bange;

nga ndi ne Katonda wange nsobola okuwalampa bbugwe.

3018:30 a Ma 32:4; Kub 15:3 b Zab 12:6 c Zab 17:7Katonda byonna by’akola bigolokofu;

Mukama ky’asuubiza akituukiriza;

era bwe buddukiro

bw’abo bonna abamwekwekamu.

3118:31 a Ma 32:39; Zab 86:8; Is 45:5, 6, 14, 18, 21 b Ma 32:31; 1Sa 2:2Kale, ani Katonda, wabula Mukama?

Era ani Lwazi, wabula Katonda waffe?

3218:32 Is 45:5Oyo ye Katonda ampa amaanyi era aluŋŋamya ekkubo lyange.

3318:33 a Kbk 3:19 b Ma 32:13Ebigere byange abinyweza ng’eby’empeewo,

n’ansobozesa okuyimirira ku ntikko z’ensozi.

3418:34 Zab 144:1Anjigiriza okulwana entalo,

ne nsobola n’okuleega omutego ogw’obusaale ogw’ekikomo.

3518:35 Zab 119:116Ompadde obulokozi bwo okuba engabo yange;

era ompaniridde n’omukono gwo ogwa ddyo;

weetoowazizza n’ongulumiza.

36Ongaziyirizza ekkubo ebigere byange we biyita,

obukongovvule bwange ne butanuuka.

3718:37 Zab 37:20; 44:5Nagoba abalabe bange embiro,

ne mbakwata ne sidda mabega okutuusa nga mbazikirizza.

3818:38 a Zab 36:12 b Zab 47:3Nababetenta ne batasobola na kugolokoka,

ne mbalinnyako ebigere byange.

39Ompadde amaanyi ag’okulwana;

abalabe bange ne banvuunamira.

4018:40 a Zab 21:12 b Zab 94:23Okyusizza abalabe bange ne bankuba amabega ne badduka,

ne ndyoka nsanyaawo abo bonna abankyawa.

4118:41 a Zab 50:22 b Yob 27:9; Nge 1:28Baalaajana naye tewaali yabawonya;

ne bakaabirira Mukama, naye n’atabaddamu.

42Ne mbamerengula ng’enfuufu empewo gy’efuumuula;

ne mbasammula eri ng’ebisooto by’omu luguudo.

4318:43 a 2Sa 8:1-14 b Is 52:15; 55:5Omponyezza obulumbaganyi bw’abantu;

n’onfuula omufuzi w’amawanga.

Abantu be nnali simanyi ne bafuuka abaweereza bange.

4418:44 Zab 66:3Olumpulira ne baŋŋondera,

bannamawanga ne bajugumira mu maaso gange.

4518:45 Mi 7:17Bannamawanga baggwaamu omutima

ne bava mu bigo byabwe nga bakankana.

4618:46 Zab 51:14Mukama mulamu! Atenderezebwe, Olwazi lwange;

era agulumizibwe Katonda w’obulokozi bwange.

4718:47 Zab 47:3Ye Katonda, asasula ku lwange abankola obubi

era akakkanya amawanga ne ngafuga.

Amponyeza abalabe bange.

4818:48 Zab 59:1Ayi Mukama, ongulumizizza okusinga abalabe bange,

n’onkuuma abakambwe ne batankwatako.

4918:49 a Zab 108:1 b Bar 15:9*Noolwekyo, Ayi Mukama, nnaakutenderezanga mu mawanga,

era nnaayimbanga nga ntendereza erinnya lyo.

5018:50 a Zab 144:10 b Zab 89:4Awa kabaka obuwanguzi obw’amaanyi,

amulaga ebyekisa emirembe gyonna oyo gwe yafukako amafuta,

eri Dawudi n’eri ezzadde lye.