Masalimo 17 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 17:1-15

Salimo 17

Pemphero la Davide.

1Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;

mverani kulira kwanga.

Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa

popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.

2Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;

maso anu aone chimene ndi cholungama.

3Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,

ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;

Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.

4Kunena za ntchito za anthu,

monga mwa mawu a pakamwa panu,

Ine ndadzisunga ndekha

posatsata njira zachiwawa.

5Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;

mapazi anga sanaterereke.

6Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;

tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.

7Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,

Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja

iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.

8Mundisunge ine ngati mwanadiso;

mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,

9kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,

kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,

ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.

11Andisaka, tsopano andizungulira

ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.

12Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;

ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;

landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.

14Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,

kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;

ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,

ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.

15Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;

pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Ketab El Hayat

مزمور 17:1-15

الْمَزْمُورُ السَّابِعَ عَشَرَ

صَلاةٌ رَفَعَهَا دَاوُدُ

1اسْمَعْ يَا رَبُّ دَعْوَى الْحَقِّ. أَنْصِتْ إِلَى صُرَاخِي، وَأَصْغِ إِلَى صَلاتِي الصَّاعِدَةِ مِنْ شَفَتَيْنِ صَادِقَتَيْنِ. 2لِيَخْرُجْ مِنْ أَمَامِكَ قَضَائِي، وَلْتُلاحِظْ عَيْنَاكَ اسْتِقَامَتِي. 3اخْتَبَرْتَ قَلْبِي إِذِ افْتَقَدْتَنِي لَيْلاً، وَامْتَحَنْتَنِي فَلَمْ تَجِدْ فِيَّ سُوءاً. لَمْ تُخَالِفْ أَقْوَالِي أَفْكَارِي. 4مَا شَأْنِي بِأَعْمَالِ النَّاسِ الشِّرِّيرَةِ؟ فَبِفَضْلِ كَلامِ شَفَتَيْكَ تَفَادَيْتُ مَسَالِكَ الْعَنِيفِ. 5ثَبَّتُّ خُطْوَاتِي فِي طُرُقِكَ فَلَمْ تَزِلَّ قَدَمَايَ.

6إِلَيْكَ دَعَوْتُ اللهُمَّ، لأَنَّكَ تَسْتَجِيبُ، فَأَرهِفْ إِلَيَّ أُذُنَكَ وَأَصْغِ لِكَلامِي. 7أَظْهِرْ رَوْعَةَ مَرَاحِمِكَ يَا مَنْ تُخَلِّصُ بِيَمِينِكَ مَنْ يَلْتَجِئُونَ إِلَيْكَ مِنْ مُطَارِدِيهِمْ. 8احْفَظْنِي كَحَدَقَةِ عَيْنِكَ، وَاسْتُرْنِي بِظِلِّ جَنَاحَيْكَ. 9احْفَظْنِي مِنَ الأَشْرَارِ الَّذِينَ يُخْرِبُونَنِي، مِنْ أَعْدَائِي الْقَتَلَةِ الْمُحْدِقِينَ بِي. 10عَوَاطِفُهُمْ مُتَحَجِّرَةٌ لَا تُشْفِقُ. أَفْوَاهُهُمْ تَنْطِقُ بِالْكِبْرِيَاءِ. 11حَاصَرُونَا مِنْ كُلِّ جِهَةٍ، وَوَطَّدُوا العَزْمَ عَلَى طَرْحِنَا أَرْضاً. 12الشِّرِّيرُ كَأَسَدٍ مُتَلَهِّفٍ لِلاِفْتِرَاسِ، وَكَالشِّبْلِ الْكَامِنِ فِي مَخْبَئِهِ. 13قُمْ يَا رَبُّ تَصَدَّ لَهُ. اصْرَعْهُ. وَبِسَيْفِكَ نَجِّ نَفْسِي مِنَ الشِّرِّيرِ. 14أَنْقِذْنِي بِيَدِكَ يَا رَبُّ مِنَ النَّاسِ. مِنْ أَهْلِ الدُّنْيَا الَّذِينَ نَصِيبُهُمْ هُوَ فِي هَذِهِ الْحَيَاةِ. أَنْتَ تَمْلَأُ بُطُونَهُمْ مِنْ خَيْرَاتِكَ الْمَخْزُونَةِ، فَيَشْبَعُ أَبْنَاؤُهُمْ، وَيُوَرِّثُونَ أَوْلادَهُمْ مَا يَفْضُلُ عَنْهُمْ. 15أَمَّا أَنَا فَبِالْبِرِّ أُشَاهِدُ وَجْهَكَ. أَشْبَعُ، إِذَا اسْتَيْقَظْتُ، مِنْ بَهَاءِ طَلْعَتِكَ.