Masalimo 17 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 17:1-15

Salimo 17

Pemphero la Davide.

1Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;

mverani kulira kwanga.

Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa

popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.

2Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;

maso anu aone chimene ndi cholungama.

3Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,

ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;

Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.

4Kunena za ntchito za anthu,

monga mwa mawu a pakamwa panu,

Ine ndadzisunga ndekha

posatsata njira zachiwawa.

5Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;

mapazi anga sanaterereke.

6Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;

tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.

7Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,

Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja

iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.

8Mundisunge ine ngati mwanadiso;

mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,

9kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,

kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,

ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.

11Andisaka, tsopano andizungulira

ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.

12Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;

ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;

landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.

14Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,

kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;

ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,

ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.

15Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;

pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 17:1-15

第 17 篇

无辜者的祈祷

大卫的祈祷。

1耶和华啊,

求你听我祈求公义的声音,

侧耳听我的呼求,

垂听我真诚的祷告。

2愿你宣判我无罪,

愿你明察是非。

3你试验过我的心思,

夜间鉴察过我,磨炼过我,

找不出任何过犯;

我立志口不犯罪。

4我遵守你的教导,洁身自守,

不与残暴之徒同流。

5我坚定地走你的道路,

从未偏离。

6上帝啊!我向你祈祷,

因为你必应允我。

求你垂听我的祷告。

7求你彰显你奇妙的慈爱,

用右手拯救投靠你的人脱离仇敌。

8求你保护我,像保护眼中的瞳仁,

用你的翅膀荫庇我,

9救我脱离恶人的攻击,

脱离四围杀气腾腾的仇敌。

10他们良心丧尽,口出狂言。

11他们穷追围堵,

伺机把我打倒在地。

12他们像急于撕碎猎物的饿狮,

又像蹲伏在暗处的猛狮。

13耶和华啊,

求你起来迎头击倒他们,

求你持刀救我脱离恶人。

14耶和华啊,

求你伸手救我脱离这些人,

脱离这些只在今生有福分的世人。

你使他们财宝无数。

他们儿女众多,

还把财富留给子孙。

15但我因持守公义必见你的面;

我醒来见到你就心满意足了。