Masalimo 16 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 16:1-11

Salimo 16

Mikitamu ya Davide.

1Ndisungeni Inu Mulungu,

pakuti ine ndimathawira kwa Inu.

2Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;

popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”

3Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,

amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.

4Anthu amene amathamangira kwa milungu ina

mavuto awo adzachulukadi.

Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi

kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.

5Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;

mwateteza kolimba gawo langa.

6Malire a malo anga akhala pabwino;

ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.

7Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;

ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.

8Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.

Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,

sindidzagwedezeka.

9Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;

thupi langanso lidzakhala pabwino,

10chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,

simudzalola kuti woyera wanu avunde.

11Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;

mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,

ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 16:1-11

第 16 篇

信靠之福

大卫的诗。

1上帝啊!我投靠你,

求你保护我。

2我对耶和华说:“你是我的主,

我美好的一切都从你而来。”

3世上敬畏你的人极其尊贵,

是我所喜爱的。

4追随假神的人,其愁苦必有增无减。

我必不向他们的假神献上血祭,

口中也不提假神的名号。

5耶和华啊,你是我的一切,

你赐我一切福分,

你掌管我的一切。

6你赐我佳美之地,

我的产业何其美!

7我要称颂赐我教诲的耶和华,

我的良心也在夜间提醒我。

8我常以耶和华为念,

祂在我右边,我必不动摇。

9因此,我的心欢喜,

我的灵快乐,

我的身体也安然无恙。

10你不会把我的灵魂撇在阴间,

也不会让你的圣者身体朽坏。

11你把生命之路指示我,

你右手有永远的福乐,

我在你面前充满喜乐。