Masalimo 150 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 150:1-6

Salimo 150

1Tamandani Yehova.

Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;

mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.

2Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;

mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.

3Mutamandeni poyimba malipenga,

mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.

4Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,

mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.

5Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,

mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.

6Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.

Tamandani Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 150:1-6

第 150 篇

赞美上帝

1你们要赞美耶和华!

在祂的圣殿赞美祂,

在彰显祂能力的穹苍赞美祂!

2你们要因祂大能的作为赞美祂,

赞美祂的无比伟大!

3要吹响号角赞美祂,

要弹琴鼓瑟赞美祂!

4要击鼓跳舞赞美祂,

要拨弦吹笛赞美祂!

5要击响铙钹赞美祂,

用响亮的钹声赞美祂!

6凡有生命的都要赞美耶和华!

你们要赞美耶和华!