Masalimo 15 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

Het Boek

Psalmen 15:1-5

1Een psalm van David.

Wie mag in uw huis wonen, Here?

Wie mag bij U zijn op uw heilige berg?

2Wie eerlijk en oprecht door het leven gaat

en altijd de waarheid spreekt.

3Wie niet kwaadspreekt,

zijn naaste geen kwaad doet

en voorkomt dat een ander wordt belasterd.

4Degene die alles wat zonde is, afwijst

en respect heeft voor wie God zoeken

en ontzag voor Hem hebben.

Als zo iemand in zijn eigen nadeel

een belofte heeft gedaan,

zal hij die toch nakomen.

5Hij zal zijn geld niet misbruiken

voor woekerpraktijken

en zich niet laten omkopen

ten koste van onschuldigen.

Wie zo door het leven gaat,

kan op Gods bescherming rekenen.