Masalimo 15 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 15:1-5

第 15 篇

安居聖山者的資格

大衛的詩。

1耶和華啊,誰能住在你的聖所?

誰能安居在你的聖山?

2就是品行純全,做事公正,

說話誠實的人。

3他不說譭謗的話,

不惡待鄰人,不造謠生事。

4他鄙視惡人,

尊重那些敬畏耶和華的人。

他起了誓,即使吃虧也不背誓。

5他不放債取利,

也不受賄去坑害無辜。

這樣的人必永遠堅立不搖。