Salimo 15
Salimo la Davide.
1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?
Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
2Munthu wa makhalidwe abwino,
amene amachita zolungama,
woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,
amene sachitira choyipa mnansi wake
kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.
Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,
amene amakwaniritsa zomwe walonjeza
ngakhale pamene zikumupweteka,
5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja
ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.
Iye amene amachita zinthu zimenezi
sadzagwedezeka konse.
De gode kan nærme sig Gud
1En sang af David.
Herre, hvem kan få adgang til din helligdom?
Hvem har lov at opholde sig hos dig på det hellige bjerg?
2De, som har et godt ry
og altid handler ret.
De, som taler sandhed af et oprigtigt hjerte
3og nægter at bagtale andre.
De, som ikke foruretter deres næste
eller taler ondt om andre.
4De, som tager afstand fra de gudløse,
men ærer dem, der adlyder Herren.
De, som holder deres løfter,
selv om det koster dem dyrt.
5De, som ikke kræver urimelige renter,
når de låner penge ud.
De, som nægter at tage imod bestikkelse
for at afgive falsk vidneudsagn.
De, som lever ret,
har intet at frygte.