Salimo 149
1Tamandani Yehova.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.
2Israeli asangalale mwa mlengi wake;
anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
3Atamande dzina lake povina
ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
4Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;
Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
5Oyera mtima asangalale mu ulemu wake
ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.
6Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,
ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
7kubwezera chilango anthu a mitundu ina,
ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
8kumanga mafumu awo ndi zingwe,
anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
9kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo
Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.
Tamandani Yehova.