Masalimo 149 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 149:1-9

Salimo 149

1Tamandani Yehova.

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.

2Israeli asangalale mwa mlengi wake;

anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.

3Atamande dzina lake povina

ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.

4Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;

Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.

5Oyera mtima asangalale mu ulemu wake

ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

6Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,

ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,

7kubwezera chilango anthu a mitundu ina,

ndi kulanga anthu a mitundu yonse,

8kumanga mafumu awo ndi zingwe,

anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,

9kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo

Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.

Tamandani Yehova.