Masalimo 148 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 148:1-14

Salimo 148

1Tamandani Yehova.

Tamandani Yehova, inu a kumwamba,

mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.

2Mutamandeni, inu angelo ake onse,

mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.

3Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,

mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.

4Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba

ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.

5Zonse zitamande dzina la Yehova

pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.

6Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;

analamula ndipo sizidzatha.

7Tamandani Yehova pa dziko lapansi,

inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,

8inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,

mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,

9inu mapiri ndi zitunda zonse,

inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,

10inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,

inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.

11Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,

inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.

12Inu anyamata ndi anamwali,

inu nkhalamba ndi ana omwe.

13Onsewo atamande dzina la Yehova

pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;

ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.

14Iye wakwezera nyanga anthu ake,

matamando a anthu ake onse oyera mtima,

Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 148:1-14

Salmo 148

1¡Aleluya! ¡Alabado sea el Señor!

Alabad al Señor desde los cielos,

alabadle desde las alturas.

2Alabadle, todos sus ángeles,

alabadle, todos sus ejércitos.

3Alabadle, sol y luna,

alabadle, estrellas luminosas.

4Alabadle vosotros, altísimos cielos,

y vosotras, las aguas que estáis sobre los cielos.

5Sea alabado el nombre del Señor,

porque él dio una orden y todo fue creado.

6Todo quedó afirmado para siempre;

emitió un decreto que no será abolido.

7Alabad al Señor desde la tierra

los monstruos marinos y las profundidades del mar,

8el relámpago y el granizo, la nieve y la neblina,

el viento tempestuoso que cumple su mandato,

9los montes y las colinas,

los árboles frutales y todos los cedros,

10los animales salvajes y los domésticos,

los reptiles y las aves,

11los reyes de la tierra y todas las naciones,

los príncipes y los gobernantes de la tierra,

12los muchachos y las muchachas,

los ancianos y los niños.

13Alabad el nombre del Señor,

porque solo su nombre es excelso;

su esplendor está por encima de la tierra y de los cielos.

14¡Él ha dado poder a su pueblo!148:14 ¡Él ha dado … su pueblo! Lit. ¡Él levantó un cuerno para su pueblo!

¡A él sea la alabanza de todos sus fieles,

de los hijos de Israel, su pueblo cercano!

¡Aleluya! ¡Alabado sea el Señor!