Masalimo 148 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 148:1-14

Salimo 148

1Tamandani Yehova.

Tamandani Yehova, inu a kumwamba,

mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.

2Mutamandeni, inu angelo ake onse,

mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.

3Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,

mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.

4Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba

ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.

5Zonse zitamande dzina la Yehova

pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.

6Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;

analamula ndipo sizidzatha.

7Tamandani Yehova pa dziko lapansi,

inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,

8inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,

mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,

9inu mapiri ndi zitunda zonse,

inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,

10inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,

inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.

11Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,

inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.

12Inu anyamata ndi anamwali,

inu nkhalamba ndi ana omwe.

13Onsewo atamande dzina la Yehova

pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;

ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.

14Iye wakwezera nyanga anthu ake,

matamando a anthu ake onse oyera mtima,

Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

Священное Писание

Забур 148:1-14

Песнь 148

1Славьте Вечного!

Славьте Вечного с небес,

в высотах прославляйте Его.

2Славьте Его, все Его ангелы,

славьте Его, все Его небесные воинства.

3Славьте Его, солнце и луна,

славьте Его, все блистающие звёзды.

4Славьте Его, небеса небес

и воды, которые выше небес148:4 См. Нач. 1:7..

5Пусть славят имя Вечного,

потому что Он повелел – и они были созданы.

6Он утвердил их навечно,

дал установление нерушимое.

7Славьте Вечного с земли,

морские чудовища и все водные глубины,

8молния и град, снег и туман,

бурный ветер, исполняющий Его слово,

9горы и все холмы,

плодовые деревья и все кедры,

10звери и всякий скот,

пресмыкающиеся и крылатые птицы,

11земные цари и все народы,

вожди и все земные правители,

12юноши и девушки,

старцы и дети –

13славьте все имя Вечного,

потому что только Его имя превознесено!

Слава Его выше земли и небес.

14Он сделал сильным148:14 Букв.: «возвысил рог». Рог был символом могущества, власти и силы. Свой народ,

прославил верных Ему –

народ Исраила, который близок Ему.

Славьте Вечного!