Masalimo 147 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 147:1-20

Salimo 147

1Tamandani Yehova.

Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,

nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!

2Yehova akumanga Yerusalemu;

Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.

3Akutsogolera anthu osweka mtima

ndi kumanga mabala awo.

4Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,

ndipo iliyonse amayitchula dzina.

5Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;

nzeru zake zilibe malire.

6Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,

koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

7Imbirani Yehova ndi mayamiko;

imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.

8Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;

amapereka mvula ku dziko lapansi

ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.

9Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe

ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.

10Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,

kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.

11Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.

12Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;

tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,

13pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako

ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.

14Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako

ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

15Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;

mawu ake amayenda mwaliwiro.

16Amagwetsa chisanu ngati ubweya

ndi kumwaza chipale ngati phulusa.

17Amagwetsa matalala ngati miyala.

Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?

18Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;

amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

19Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,

malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.

20Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;

anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 147:1-20

第 147 篇

赞美上帝复兴耶路撒冷

1你们要赞美耶和华!

歌颂我们的上帝,真是美好!

赞美祂,真是快乐合宜!

2耶和华重建耶路撒冷

召集被掳去的以色列人。

3祂医治心灵破碎的人,

包扎他们的创伤。

4祂决定众星的数目,

给它们一一命名。

5我们的主伟大无比,充满力量,

祂的智慧没有穷尽。

6耶和华扶持谦卑人,

毁灭邪恶人。

7你们要以感恩的心歌颂耶和华,

弹琴赞美我们的上帝。

8祂以云霞遮蔽天空,

降雨水滋润大地,

使山上长出绿草。

9祂赐食物给走兽,

喂养嗷嗷待哺的小乌鸦。

10耶和华所喜悦的不是强健的马匹,

也不是矫捷的战士,

11而是敬畏祂、仰望祂慈爱的人。

12耶路撒冷啊,要颂赞耶和华;

锡安啊,要赞美你的上帝。

13因为祂使你的城门坚固,

赐福给你的儿女。

14祂使你四境平安,

饱享上好的麦子。

15祂向大地发出命令,

祂的话迅速传开。

16祂降下羊毛般的白雪,

撒下炉灰般的寒霜。

17祂抛下碎石般的冰雹,

谁能经得住祂降下的严寒呢?

18祂一声令下,冰雪便溶化,

微风便吹拂,河川便奔流。

19祂将自己的话传于雅各

将自己的律例和法令指示以色列

20祂未曾这样对待其他国家,

他们不知道祂的律法。

你们要赞美耶和华!