Masalimo 146 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 146:1-10

Salimo 146

1Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

2Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

3Musamadalire mafumu,

anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

4Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;

zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

5Wodala ndi amene thandizo lake ndi

Mulungu wa Yakobo.

6Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;

Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.

7Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa

ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Yehova amamasula amʼndende,

8Yehova amatsekula maso anthu osaona,

Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,

Yehova amakonda anthu olungama.

9Yehova amasamalira alendo

ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,

koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 146:1-10

第 146 篇

讚美上帝的幫助

1你們要讚美耶和華!

我的心啊,你要讚美耶和華。

2我要一生讚美耶和華,

我一息尚存都要讚美祂。

3你們不要倚靠權貴,

不要倚靠世人,

他們救不了你們。

4他們氣息一斷,便歸回塵土,

他們的打算轉眼成空。

5雅各的上帝相助、仰望上帝耶和華的人有福了!

6耶和華創造了天、地、海和其中的萬物,

祂永遠信實可靠。

7祂為受壓制的人伸冤,

賜食物給饑餓的人,

使被囚者得自由。

8耶和華叫瞎子看見,

扶持被重擔所壓的人,

祂喜愛義人。

9耶和華保護寄居異地的人,

看顧孤兒寡婦,

祂挫敗惡人的陰謀詭計。

10耶和華永遠掌權。

錫安啊,

你的上帝要世世代代做王。

你們要讚美耶和華!