Masalimo 145 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 145:1-21

Salimo 145

Salimo la matamando la Davide.

1Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;

ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku

ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;

ukulu wake palibe angawumvetsetse.

4Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;

Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.

5Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,

ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

6Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,

ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.

7Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,

ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

8Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

9Yehova ndi wabwino kwa onse;

amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.

10Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;

oyera mtima adzakulemekezani.

11Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu

ndi kuyankhula za mphamvu yanu,

12kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu

ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.

13Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,

ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse

ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.

14Yehova amagwiriziza onse amene akugwa

ndipo amakweza onse otsitsidwa.

15Maso a onse amayangʼana kwa Inu,

ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.

16Mumatsekula dzanja lanu

ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,

ndi wokonda zonse zimene anazipanga.

18Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

19Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;

amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.

20Yehova amayangʼana onse amene amamukonda

koma adzawononga anthu onse oyipa.

21Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.

Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera

ku nthawi za nthawi.

O Livro

Salmos 145:1-21

Salmo 145

Salmo de David.

1Eu te louvarei, meu Deus e meu Rei!

Quero cantar a força do teu nome para sempre!

2Sim, dia após dia, quero louvar-te

e por toda a eternidade

falar de toda a grandeza do teu nome.

3Grande é o Senhor

e inteiramente digno de louvor;

a sua grandeza ultrapassa o nosso entendimento.

4Cada geração conte aos seus descendentes

as maravilhas que o Senhor faz.

5Quero falar da magnífica glória da tua majestade

e meditar nas tuas maravilhas.

6Toda a fama dos teus espantosos milagres

correrá de boca em boca,

assim como toda a tua grandeza.

7Todos falarão da tua bondade

e cantarão a tua justiça.

8Bondoso e misericordioso é o Senhor;

ele é paciente e cheio de amor.

9É bom para todos;

tudo o que faz é consequência do seu amor.

10Tudo o que criaste, Senhor, é motivo

para que aqueles que te pertencem te louvem.

11Para que falem da glória do teu reino,

mencionando os feitos do teu poder.

12Darão a conhecer à humanidade os teus milagres,

a tua majestade e a glória do teu reino.

13O teu reino não tem fim;

o teu domínio estende-se por todas as gerações.

14O Senhor ampara todos os que caem

e levanta os que estão abatidos.

15Os olhos de todos estão postos em ti, Senhor;

tu lhes dás alimento conforme o que precisam.

16Abres a tua generosa mão

e satisfazes os desejos de todo o ser vivo.

17Justo é o Senhor em tudo o que faz;

as suas obras têm a marca da sua bondade.

18O Senhor está perto de todos os que o chamam,

de todos os que o invocam em verdade.

19Realizará os desejos daqueles que o temem;

ouvirá os seus apelos e os salvará.

20O Senhor guarda todos os que o amam,

mas todos os ímpios serão destruídos.

21Louvarei o Senhor, publicamente,

e todos os habitantes da Terra louvarão

a força do seu nome, para sempre!