Masalimo 145 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 145:1-21

Salimo 145

Salimo la matamando la Davide.

1Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;

ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku

ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;

ukulu wake palibe angawumvetsetse.

4Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;

Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.

5Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,

ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

6Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,

ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.

7Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,

ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

8Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

9Yehova ndi wabwino kwa onse;

amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.

10Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;

oyera mtima adzakulemekezani.

11Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu

ndi kuyankhula za mphamvu yanu,

12kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu

ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.

13Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,

ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse

ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.

14Yehova amagwiriziza onse amene akugwa

ndipo amakweza onse otsitsidwa.

15Maso a onse amayangʼana kwa Inu,

ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.

16Mumatsekula dzanja lanu

ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,

ndi wokonda zonse zimene anazipanga.

18Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

19Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;

amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.

20Yehova amayangʼana onse amene amamukonda

koma adzawononga anthu onse oyipa.

21Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.

Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera

ku nthawi za nthawi.

Het Boek

Psalmen 145:1-21

1Een loflied van David.

Mijn God, ik zal U roemen.

U bent mijn Koning.

Uw naam wil ik mijn leven lang loven.

2Elke dag zal ik U eren

en uw naam prijzen zolang ik leef.

3De Here is een grote God

en Hem komt alle eer toe.

Voor ons mensen is niet te begrijpen

hoe groot Hij is.

4Van generatie op generatie

zal men U prijzen om wat U doet.

Men zal dan vertellen

over uw grote daden.

5Ik wil vertellen

over uw geweldige heerlijkheid

en uw machtige wonderen.

6Die gaan over uw macht en roem.

Ik wil vertellen hoe groot U bent.

7Laat uw grote goedheid geroemd worden

en juichende liederen worden gezongen

over uw rechtvaardigheid.

8De Here geeft genade

en ontfermt Zich liefdevol.

Hij heeft een onmetelijk geduld

en is groot in zijn goedheid en liefde.

9De Here is goed voor iedereen

en vol liefde ontfermt Hij Zich

over alles wat Hij heeft gemaakt.

10Alles wat U hebt gemaakt,

prijst U, Here.

Ook allen die U liefhebt,

zullen U loven.

11Zij vertellen over uw goddelijk koningschap

en over uw grote macht.

12Zo zullen alle mensen horen

over uw grote daden

en over de geweldige majesteit van uw koningschap.

13Uw koningschap is eeuwig,

U heerst over elke generatie.

14De Here ondersteunt

ieder die dreigt te vallen.

Ieder die gebukt gaat,

helpt Hij overeind.

15Alle ogen zijn op U gericht,

U voorziet ieder op zijn tijd van voedsel.

16Als U uw hand opendoet,

maakt U iedereen gelukkig.

17De Here is rechtvaardig

in alles wat Hij doet.

Zijn goedheid en liefde stralen af

van alles wat Hij maakt.

18De Here is dichtbij ieder

die Hem aanroept met een zuiver hart.

19Mensen die ontzag voor Hem hebben,

komt Hij tegemoet.

Hij hoort hun roepen om hulp en redt hen.

20De Here zorgt voor ieder

die van Hem houdt,

maar Hij vernietigt de ongelovigen.

21Zonder ophouden wil ik vertellen

over de grootheid van de Here.

Tot in de eeuwigheid zal alles wat leeft

zijn heilige naam eren.