Masalimo 145 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 145:1-21

Salimo 145

Salimo la matamando la Davide.

1Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;

ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku

ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;

ukulu wake palibe angawumvetsetse.

4Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;

Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.

5Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,

ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

6Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,

ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.

7Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,

ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

8Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

9Yehova ndi wabwino kwa onse;

amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.

10Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;

oyera mtima adzakulemekezani.

11Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu

ndi kuyankhula za mphamvu yanu,

12kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu

ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.

13Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,

ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse

ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.

14Yehova amagwiriziza onse amene akugwa

ndipo amakweza onse otsitsidwa.

15Maso a onse amayangʼana kwa Inu,

ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.

16Mumatsekula dzanja lanu

ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,

ndi wokonda zonse zimene anazipanga.

18Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

19Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;

amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.

20Yehova amayangʼana onse amene amamukonda

koma adzawononga anthu onse oyipa.

21Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.

Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera

ku nthawi za nthawi.

Hoffnung für Alle

Psalm 145:1-21

Gottes Liebe ist grenzenlos

1Ein Loblied von David.

Dich will ich ehren, mein Gott und König,

deinen Namen will ich preisen für alle Zeit!

2Jeden Tag will ich Gutes von dir reden

und deinen Namen für immer loben!

3Groß ist der Herr! Jeder soll ihn rühmen!

Seine Größe kann niemand erfassen.

4Eine Generation soll der anderen von deinen Taten erzählen

und schildern, wie machtvoll du eingegriffen hast.

5Deine Pracht und Herrlichkeit wird in aller Munde sein,

und auch ich will stets über deine Wunder nachdenken.

6Immer wieder wird man davon sprechen,

wie ehrfurchtgebietend dein Handeln ist.

Auch ich will verkünden, welche gewaltigen Taten du vollbringst.

7Wenn die Menschen deines Volkes zurückdenken,

werden sie deine unermessliche Güte besingen.

Über deine Gerechtigkeit werden sie jubeln und rufen:

8»Gnädig und barmherzig ist der Herr;

groß ist seine Geduld und grenzenlos seine Liebe!

9Der Herr ist gut zu allen

und schließt niemanden von seinem Erbarmen aus,

denn er hat allen das Leben gegeben.«

10Darum sollen dich alle deine Geschöpfe loben.

Jeder, der dir die Treue hält, soll dich rühmen

11und weitersagen, wie großartig dein Königtum ist!

Sie alle sollen erzählen von deiner Stärke,

12damit die Menschen von deinen gewaltigen Taten erfahren

und von der herrlichen Pracht deines Reiches!

13Deine Herrschaft hat kein Ende,

von einer Generation zur nächsten bleibt sie bestehen.

Auf das Wort des Herrn kann man sich verlassen,

und was er tut, das tut er aus Liebe.145,13 Vers 13b ist eine Ergänzung nach einigen alten Handschriften und Übersetzungen.

14Wer keinen Halt mehr hat, den hält der Herr;

und wer am Boden liegt, den richtet er wieder auf.

15Alle schauen erwartungsvoll zu dir,

und du gibst ihnen zu essen zur rechten Zeit.

16Du öffnest deine Hand und sättigst deine Geschöpfe;

allen gibst du, was sie brauchen.

17Der Herr ist gerecht in allem, was er tut;

auf ihn ist immer Verlass!

18Der Herr ist denen nahe,

die zu ihm beten und es ehrlich meinen.

19Er erfüllt die Bitten der Menschen, die voll Ehrfurcht zu ihm kommen.

Er hört ihren Hilfeschrei und rettet sie.

20Der Herr bewahrt alle, die ihn lieben,

aber wer mit ihm nichts zu tun haben will, den lässt er umkommen.

21Ich will den Herrn loben,

und alles, was lebt, soll seinen heiligen Namen preisen,

jetzt und für alle Zeit!