Masalimo 144 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Nueva Versión Internacional

Salmo 144:1-15

Salmo 144

Salmo de David.

1Bendito sea el Señor, mi Roca,

que adiestra mis manos para la guerra,

mis dedos para la batalla.

2Él es mi Dios amoroso, mi amparo,

mi más alto escondite, mi libertador,

mi escudo, en quien me refugio.

Él es quien pone los pueblos144:2 los pueblos (Targum, Vulgata, Siríaca, Aquila y varios mss. hebreos); mi pueblo (TM). a mis pies.

3Señor, ¿qué es el ser humano para que lo cuides?

¿Qué es el simple mortal para que en él pienses?

4Todo ser humano es como un suspiro;

sus días son fugaces como una sombra.

5Abre tus cielos, Señor, y desciende;

toca los montes y haz que echen humo.

6Lanza relámpagos y dispersa al enemigo;

dispara tus flechas y confúndelos.

7Extiende tu mano desde las alturas

y sálvame de las aguas tumultuosas;

líbrame del poder de gente extraña.

8Cuando abren la boca, dicen mentiras;

cuando levantan su diestra, juran con falsedad.144:8 cuando … con falsedad. Lit. su diestra es diestra de engaño; también en v. 11.

9Te cantaré, oh Dios, un cántico nuevo;

con la lira de diez cuerdas te cantaré salmos.

10Tú das la victoria a los reyes;

a tu siervo David lo libras de la espada mortal.

11Ponme a salvo,

líbrame del poder de gente extraña.

Cuando abren la boca, dicen mentiras;

cuando levantan su diestra, juran con falsedad.

12Que nuestros hijos, en su juventud,

crezcan como plantas frondosas;

que sean nuestras hijas como columnas esculpidas

para adornar un palacio.

13Que nuestros graneros se llenen

con provisiones de toda especie.

Que nuestros rebaños aumenten por millares,

por decenas de millares en nuestros campos.

14Que nuestros bueyes arrastren cargas pesadas;144:14 Que nuestros … cargas pesadas. Alt. Que nuestros capitanes sean establecidos firmemente.

que no haya brechas ni salidas,

ni gritos de angustia en nuestras calles.

15¡Dichoso el pueblo que recibe todo esto!

¡Dichoso el pueblo cuyo Dios es el Señor!