Masalimo 144 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 144:1-15

Псалам 144

Давидов.

1Благословен да је Господ, стена моја,

што ми руке за рат

и прсте за борбу увежбава;

2милосрђе моје и тврђава моја;

моје уточиште и мој избавитељ;

мој штит, онај у коме уточиште налазим

и који ми мој народ покорава.

3О, Господе, шта је човек да за њега мариш

и људски потомак да се са њим бавиш?

4Човек тек је даху налик

и дани му бледе као сенка.

5О, Господе, небеса своја спусти, па да сиђеш

и дотакнеш брда да се пуше!

6Засевај муњом,

нека се распрше!

Стреле своје баци,

нека се разбеже!

7Са висина руке пружи,

избави ме;

извади ме из бујица

и из руку деце туђинаца;

8оних што устима својим обмањују

и десницом својом заклињу се лажно.

9О, Боже, певаћу ти нову песму,

на лири са десет струна ја свираћу теби;

10теби који царевима избављење дајеш;

који Давида, слугу свога,

спасаваш од мача опакога.

11Ослободи ме, избави ме

из руке деце туђинаца,

оних што устима својим обмањују

и десницом својом заклињу се лажно.

12Тад синови наши нека буду

као стабло горостасно у младости својој;

наше ћерке нека буду

попут шара стубова палате.

13Амбари ће наши бити пуни

разноврсног рода;

хиљаде ће ојагњити овце наше,

и десет хиљада по пашњацима нашим.

14Волови ће теглити, неће бити разарања,

неће бити бежаније

и вриска се неће чути

по трговима нашим.

15Благо народу коме тако буде!

Благо народу коме Бог је Господ!