Masalimo 144 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Japanese Contemporary Bible

詩篇 144:1-15

144

1揺るぎない岩である主をほめたたえます。

戦いが起こると、主は、

弓をひく私の腕を強めてくださいます。

2いつも恵み深く、愛を注いでくださる主は、

私の要塞であり、びくともしないやぐらです。

私を救ってくださる神は、

盾となって立ちはだかってくださいます。

こうして、神は

民を私に服従させてくださるのです。

3主よ。あなたが気に留めてくださるのは、

人間が何者だからなのでしょう。

どうしてあなたは、

こんな人間にかかわってくださるのでしょう。

4人の一生は、ただのひと呼吸のよう、

また影のようで、はかなく消えるではありませんか。

5主よ、どうか、天を押し曲げて降りて来てください。

あなたの手が山に触れると、煙が吹き出します。

6主よ、いなずまの矢を敵に放ち、

彼らを散らすように蹴散らしてください。

7天から御手を差し伸べ、私を引き上げてください。

深い水の中から、強い敵の腕から、

助け出してください。

8彼らの口はうそで満ち、

間違っていることをほんとうだと言い張ります。

9ああ神よ。私は十弦の琴をかなで、

あなたに新しい歌をささげます。

10あなたは王に勝利をもたらされるお方です。

あなたのしもべダビデを、

悪の剣から救い出されるお方です。

11どうか、悪賢い敵から、私を救い出してください。

12-15神を信じる国の祝福された様子を語りましょう。

男の子は、すくすくと成長する木のように、

元気いっぱいに育ちます。

女の子は、宮殿にふさわしく飾られた柱のように、

しとやかで優雅です。

倉には穀物がこれ以上入らないほど

豊かにあります。

羊の群れは、何千頭、何万頭と増え、

牛は次々と子どもを産みます。

敵は一人も攻めて来ず、平和が満ちあふれています。

町には一つの犯罪も起こりません。

このように、主を神とする民は幸いです。