Masalimo 143 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.

New Serbian Translation

Псалми 143:1-12

Псалам 143

Псалам Давидов.

1О, Господе, чуј молитву моју

и послушај преклињања моја!

Услиши ме по верности,

по праведности својој.

2Са слугом својим немој на суд ићи,

јер пред тобом нема живог,

а да је праведан.

3Јер душманин душу моју гони,

живог ме о земљу ломи;

тера ме да живим по мрачним местима,

као оне што су одавно покојни.

4Клонуо је дух мој у мени,

срце ми је уцвељено у грудима!

5Прохујалих дана присећам се,

уносим се у сва твоја дела

и разматрам дело твојих руку.

6Руке своје к теби ширим,

душа моја те је жедна

као земља сува. Села

7Пожури се, услиши ме!

О, Господе, дух мој копни!

Лице своје од мене не скривај,

да не будем попут оних што иду у раку.

8Кад је јутро објави ми своју милост,

јер у тебе уздајем се;

објави ми пут којим ћу поћи

јер је моја душа тебе жељна.

9О, Господе, избави ме од душмана мојих!

К теби бежим да се скријем.

10Поучи ме да по твојој вољи чиним,

јер Бог мој ти си;

ти си доброг духа,

поведи ме где је земља равна.

11О, Господе, због имена свога

сачувај ме живог!

Праведношћу својом душу моју

од невоље спаси.

12По милости својој

затри противнике моје;

искорени све душмане душе моје,

јер ја сам твој слуга!