Masalimo 143 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.

New Russian Translation

Псалтирь 143:1-15

Псалом 143

1Псалом Давида.

Благословен будь Господь, скала моя,

обучающий мои руки войне

и мои пальцы – битве.

2Он – милость моя и крепость моя,

прибежище мое и избавитель мой, щит мой,

Тот, на Кого я уповаю,

Кто подчиняет мне мой народ143:2 Или: народы..

3Господи, кто такой человек, что Ты знаешь о нем,

и сын человеческий, что Ты обращаешь на него внимание?

4Человек подобен дуновению ветра;

дни его – как уходящая тень.

5Господи, приклони небеса и сойди;

коснись гор – и задымятся они.

6Брось молнию и рассей их,

выпусти Свои стрелы и смети их.

7Протяни руку Свою с высоты;

избавь меня и спаси

от великих вод,

от рук чужеземцев,

8чьи уста говорят неправду

и чья правая рука полна обмана.

9Новую песню воспою Тебе, Боже,

на десятиструнной лире сыграю Тебе –

10Тому, Кто дает победу143:10 Или: спасение. царям,

избавляет Давида, Своего слугу,

от смертоносного меча.

11Избавь меня и спаси

от рук чужеземцев,

чьи уста говорят неправду

и чья правая рука полна обмана.

12Пусть будут наши сыновья

подобны молодым разросшимся растениям;

пусть будут наши дочери

подобны стройным колоннам во дворцах;

13да будут наши житницы полны,

богаты всяким зерном;

да будут на наших пастбищах

тысячи, десятки тысяч овец;

14да будут жиреть наши волы;

да не будет ни расхищения, ни пропажи,

ни воплей на наших улицах.

15Блажен тот народ, у которого все так и есть;

блажен тот народ, чей Бог – Господь!