Masalimo 143 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.

Hoffnung für Alle

Psalm 143:1-12

Bring mich nicht vor dein Gericht!

1Ein Lied von David.

Herr, höre mein Gebet!

Achte auf mein Flehen und hilf mir,

du bist doch treu und gerecht!

2Bring mich nicht vor dein Gericht,

denn vor dir ist kein Mensch unschuldig.

3Der Feind verfolgt mich

und wirft mich zu Boden.

In völliger Dunkelheit lässt er mich zurück,

als wäre ich schon lange tot.

4Ich weiß nicht mehr weiter

und bin vor Angst wie gelähmt.

5Ich denke zurück an früher, an das, was du damals getan hast,

und halte mir deine großen Taten vor Augen.

6Zu dir strecke ich meine Hände empor im Gebet.

Wie ausgedörrtes Land nach Regen lechzt,

so warte ich sehnsüchtig auf dein Eingreifen.

7Herr, erhöre mich doch jetzt –

ich bin völlig am Ende!

Verbirg dich nicht vor mir,

sonst habe ich nicht mehr lange zu leben!

8Lass mich schon früh am Morgen erfahren,

dass du es gut mit mir meinst,

denn ich vertraue dir.

Zeige mir, wohin ich gehen soll,

denn nach dir sehne ich mich.

9Rette mich, Herr, vor meinen Feinden –

nur bei dir bin ich geborgen.

10Lehre mich, so zu leben, wie du es willst,

denn du bist mein Gott!

Führe mich durch deinen guten Geist,

dann kann ich ungehindert meinen Weg gehen!

11Herr, ich weiß, du bist gerecht, darum hilf mir aus meiner Not!

Es wird deinem Namen Ehre machen, wenn du mich am Leben erhältst.

12Lass meine Feinde umkommen

und vernichte alle, die mich verfolgen!

Denn du bist ein gnädiger Gott, und ich diene dir.