Masalimo 142 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 142:1-7

Salimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

1Ndikulirira Yehova mofuwula;

ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.

2Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;

ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

3Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,

ndinu amene mudziwa njira yanga.

Mʼnjira imene ndimayendamo

anthu anditchera msampha mobisa.

4Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;

palibe amene akukhudzika nane.

Ndilibe pothawira;

palibe amene amasamala za moyo wanga.

5Ndilirira Inu Yehova;

ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,

gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”

6Mverani kulira kwanga

pakuti ndathedwa nzeru;

pulumutseni kwa amene akundithamangitsa

pakuti ndi amphamvu kuposa ine.

7Tulutseni mʼndende yanga

kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira

chifukwa cha zabwino zanu pa ine.