Salimo 142
Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.
1Ndikulirira Yehova mofuwula;
ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.
2Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;
ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.
3Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,
ndinu amene mudziwa njira yanga.
Mʼnjira imene ndimayendamo
anthu anditchera msampha mobisa.
4Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;
palibe amene akukhudzika nane.
Ndilibe pothawira;
palibe amene amasamala za moyo wanga.
5Ndilirira Inu Yehova;
ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,
gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”
6Mverani kulira kwanga
pakuti ndathedwa nzeru;
pulumutseni kwa amene akundithamangitsa
pakuti ndi amphamvu kuposa ine.
7Tulutseni mʼndende yanga
kuti nditamande dzina lanu.
Ndipo anthu olungama adzandizungulira
chifukwa cha zabwino zanu pa ine.
الْمَزْمُورُ الْمِئَةُ وَالثَّانِي وَالأَرْبَعُونَ
قَصِيدَةٌ لِدَاوُدَ عِنْدَمَا كَانَ مُخْتَبِئاً فِي الْمَغَارَةِ. صَلاةٌ
1بِصَوْتِي إِلَى الرَّبِ أَصْرُخُ. بِصَوْتِي إِلَى الرَّبِّ أَتَضَرَّعُ. 2أَبُثُّهُ شَكْوَايَ وَأُحَدِّثُهُ بِضِيقِي. 3عِنْدَمَا غُشِيَ عَلَى رُوحِي فِي دَاخِلِي كُنْتَ أَنْتَ عَالِماً بِمَسْلَكِي. فِي الطَّرِيقِ الَّتِي سَلَكْتُهَا نَصَبُوا لِي فَخّاً. 4الْتَفِتْ نَحْوَ يَمِينِي فَلَا تَجِدَ مَنْ يَحْفَلُ بِي، لَمْ يَبْقَ لِي مَلاذٌ أَوْ مَنْ يَسْأَلُ عَنِّي. 5إِيَّاكَ دَعَوْتُ يَا رَبُّ قَائِلاً: «أَنْتَ مَلْجَإِي، أَنْتَ نَصِيبِي فِي أَرْضِ الأَحْيَاءِ». 6أَصْغِ إِلَى صُرَاخِي لأَنَّنِي قَدْ تَذَلَّلْتُ جِدّاً. أَنْقِذْنِي مِنْ مُضْطَهِدِيَّ لأَنَّهُمْ أَشَدُّ مِنِّي. 7أَفْرِجْ كُرْبَةَ نَفْسِي لأُسَبِّحَ بِاسْمِكَ، فَيَلْتَفَّ الصِّدِّيقُونَ حَوْلِي ثَوَاباً لِي مِنْكَ.