Masalimo 142 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 142:1-7

Salimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

1Ndikulirira Yehova mofuwula;

ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.

2Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;

ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

3Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,

ndinu amene mudziwa njira yanga.

Mʼnjira imene ndimayendamo

anthu anditchera msampha mobisa.

4Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;

palibe amene akukhudzika nane.

Ndilibe pothawira;

palibe amene amasamala za moyo wanga.

5Ndilirira Inu Yehova;

ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,

gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”

6Mverani kulira kwanga

pakuti ndathedwa nzeru;

pulumutseni kwa amene akundithamangitsa

pakuti ndi amphamvu kuposa ine.

7Tulutseni mʼndende yanga

kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira

chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Korean Living Bible

시편 142:1-7

어려움에 처했을 때

(다윗의 교훈시. 그가 굴에 숨어 있을 때 지은 노래)

1내가 여호와께

큰 소리로 부르짖고

간구합니다.

2내가 억울한 사정을

주 앞에 털어놓고

나의 모든 어려움을

주께 말합니다.

3내가 이처럼 위축되어

절망하고 있을 때

나의 갈 길을 아시는 분은

주밖에 없습니다.

내 원수들이 나를 잡으려고

덫을 놓았습니다.

4내 오른편을 살펴보소서.

나를 돕거나 보호하는 자도 없고

나를 보살펴 주는 자도 없습니다.

5여호와여,

내가 주께 부르짖습니다.

주는 나의 피난처이시며

142:5 또는 ‘생존 세계에서 나의 분깃이시라’내가 이 세상에서

필요로 하는 전체입니다.

6나의 부르짖음을 들으소서.

내가 말할 수 없는

어려움에 처해 있습니다.

추격하는 자들에게서

나를 구하소서.

그들은 나보다 강합니다.

7내 영혼을 감옥에서 끌어내어

주의 이름을 찬양하게 하소서.

주께서 나에게

은혜를 베푸실 것이므로

의로운 자들이

내 주변에 모여들 것입니다.