Masalimo 141 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

New International Version

Psalms 141:1-10

Psalm 141

A psalm of David.

1I call to you, Lord, come quickly to me;

hear me when I call to you.

2May my prayer be set before you like incense;

may the lifting up of my hands be like the evening sacrifice.

3Set a guard over my mouth, Lord;

keep watch over the door of my lips.

4Do not let my heart be drawn to what is evil

so that I take part in wicked deeds

along with those who are evildoers;

do not let me eat their delicacies.

5Let a righteous man strike me—that is a kindness;

let him rebuke me—that is oil on my head.

My head will not refuse it,

for my prayer will still be against the deeds of evildoers.

6Their rulers will be thrown down from the cliffs,

and the wicked will learn that my words were well spoken.

7They will say, “As one plows and breaks up the earth,

so our bones have been scattered at the mouth of the grave.”

8But my eyes are fixed on you, Sovereign Lord;

in you I take refuge—do not give me over to death.

9Keep me safe from the traps set by evildoers,

from the snares they have laid for me.

10Let the wicked fall into their own nets,

while I pass by in safety.