Masalimo 141 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

Korean Living Bible

시편 141:1-10

악에 빠지지 않게 하소서

(다윗의 시)

1여호와여,

내가 주께 부르짖습니다.

속히 나에게 오셔서

내가 부르짖을 때

내 음성에 귀를 기울이소서.

2나의 기도를 주께 드리는

향과 저녁 제사처럼 받으소서.

3여호와여, 내 입에

경비병을 세우시고

내 입술의 문을 지키소서.

4내 마음이 악한 것에 끌려

악을 행하는 자들과 함께

악한 짓을 하지 않게 하시고

그들의 잔치에

참석하지 않게 하소서.

5의로운 자들이

나를 치고 책망할지라도

내가 그것을 좋게 여기고

거절하지 않을 것이나

141:5 또는 ‘저희의 재난 중에라도 내가 항상 기도하리로다’악인들의 악한 행위는

내가 대적하고

항상 기도하리라.

6그들의 통치자들이

바위 절벽에서 떨어질 때

사람들은

내 말을 들을 것이다.

7사람들이 밭을 갈아

흙덩이를 부수뜨려 놓은 것처럼

우리 뼈가 141:7 또는 ‘음부 문에’무덤가에 흩어졌구나.

8주 여호와여,

내가 주를 바라보며

주를 신뢰합니다.

나를 죽도록 내버려 두지 마소서.

9나를 지키셔서

악인들의 덫과 함정에

걸려들지 않게 하소서.

10그들을

자기 그물에 걸리게 하시고

나는 무사히 피하게 하소서.