Salimo 140
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;
tetezeni kwa anthu ankhanza,
2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa
ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;
pa milomo yawo pali ululu wa mamba.
Sela
4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;
tchinjirizeni kwa anthu ankhanza
amene amakonza zokola mapazi anga.
5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;
iwo atchera zingwe za maukonde awo
ndipo anditchera misampha pa njira yanga.
Sela
6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
Imvani kupempha kwanga Yehova.
7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,
mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;
musalole kuti zokonza zawo zitheke,
mwina iwo adzayamba kunyada.
Sela
9Mitu ya amene andizungulira
iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10Makala amoto agwere pa iwo;
aponyedwe pa moto,
mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;
choyipa chilondole anthu ankhanza.
12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,
ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,
ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Псалам 140
Хоровођи. Давидов Псалам.
1О, Господе, избави ме од човека злобног,
од човека насилника ти мене заштити;
2оног што му срце злобу смишља,
оних што поваздан започињу свађе.
3Попут змије оштре језик,
отров им је змијски под уснама. Села
4Заштити ме, о, Господе,
од шака поквареног,
од човека насилника ти мене заштити
и од оних што би да ме са ногу помету.
5Охоли су ми замку и омче сакрили,
крај пута ми мрежу раширили
и клопке ставили. Села
6Господу говорим: „Бог мој ти си!“
О, Господе, пригни ухо гласу мојих преклињања!
7О, Господе Боже, сило мог спасења,
у дан ратни главу моју покриј.
8О, Господе, не дај злобном по жељама;
злу намеру му не оствари, да се не охоли. Села
9Ено глава оних што ме окружују!
Зло усана њихових нек се на њих сручи!
10Нека на њих падне жар угљени;
у ватру нека их гурне,
у раке, и нек се не дигну!
11Нека се клеветник не укорени на земљи;
насилника нека злоба лови,
нека га надвлада.
12А ја знам да ће Господ суд донети сиромаху
и правду за убогога!
13Нек праведни хвале твоје име!
Честити ће пред тобом живети!