Masalimo 140 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 140:1-13

Salimo 140

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;

tetezeni kwa anthu ankhanza,

2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa

ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.

3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;

pa milomo yawo pali ululu wa mamba.

Sela

4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;

tchinjirizeni kwa anthu ankhanza

amene amakonza zokola mapazi anga.

5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;

iwo atchera zingwe za maukonde awo

ndipo anditchera misampha pa njira yanga.

Sela

6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

Imvani kupempha kwanga Yehova.

7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,

mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.

8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;

musalole kuti zokonza zawo zitheke,

mwina iwo adzayamba kunyada.

Sela

9Mitu ya amene andizungulira

iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.

10Makala amoto agwere pa iwo;

aponyedwe pa moto,

mʼmaenje amatope, asatulukemonso.

11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;

choyipa chilondole anthu ankhanza.

12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,

ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.

13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,

ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Hoffnung für Alle

Psalm 140:1-14

Hinterlistige Feinde

1Ein Lied von David.

2Herr, rette mich vor bösen Menschen!

Beschütze mich vor denen, die sich mit roher Gewalt durchsetzen!

3Ständig brüten sie Gemeinheiten aus

und versuchen, Streit anzufangen.

4Sie reden mit spitzer Zunge,

und was über ihre Lippen kommt,

ist bösartig und todbringend wie Schlangengift.

5-6Herr, lass nicht zu,

dass ich in die Hände der Gottlosen gerate!

Verschone mich vor diesen überheblichen Leuten,

die mich um jeden Preis zu Fall bringen wollen!

Heimlich haben sie mir Fallen gestellt,

auf allen Wegen lauert die Gefahr.

7Ich aber sage: Herr, du bist mein Gott!

Höre mich, wenn ich zu dir um Hilfe rufe!

8Herr, mein Gott, schon oft warst du meine Rettung.

Als der Kampf um mich tobte, hast du mich beschützt.

9So hilf mir auch jetzt: Durchkreuze die Pläne der Unheilstifter,

lass ihre bösen Vorhaben misslingen,

damit sie nicht noch überheblicher werden!

10Lass sie selbst von dem Leid überwältigt werden,

das sie mir zufügen wollten!

11Sprich ihnen das Urteil: Lass glühende Kohlen auf sie fallen,

stürze sie ins Feuer, in tiefe Schluchten,

aus denen sie nicht mehr entkommen können!

12Wer den guten Ruf eines anderen zerstört,

der soll in diesem Land kein Glück haben.

Und wer vor brutaler Gewalt nicht zurückschreckt,

der soll vom Unglück verfolgt werden.

13Ich weiß, dass der Herr den Unterdrückten beisteht

und den Wehrlosen zu ihrem Recht verhilft.

14Deshalb werden dich, Herr, alle preisen, die zu dir gehören.

Deine Nähe erfährt jeder, der aufrichtig mit dir lebt.