Masalimo 140 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 140:1-13

Salimo 140

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;

tetezeni kwa anthu ankhanza,

2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa

ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.

3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;

pa milomo yawo pali ululu wa mamba.

Sela

4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;

tchinjirizeni kwa anthu ankhanza

amene amakonza zokola mapazi anga.

5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;

iwo atchera zingwe za maukonde awo

ndipo anditchera misampha pa njira yanga.

Sela

6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

Imvani kupempha kwanga Yehova.

7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,

mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.

8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;

musalole kuti zokonza zawo zitheke,

mwina iwo adzayamba kunyada.

Sela

9Mitu ya amene andizungulira

iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.

10Makala amoto agwere pa iwo;

aponyedwe pa moto,

mʼmaenje amatope, asatulukemonso.

11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;

choyipa chilondole anthu ankhanza.

12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,

ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.

13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,

ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 140:1-13

第 140 篇

祈求上帝保護

大衛的詩,交給樂長。

1耶和華啊!

求你拯救我脫離惡人,

保護我脫離殘暴之徒。

2他們心懷叵測,整天挑撥離間。

3他們的言語惡毒如蛇,

嘴唇有蛇的毒液。(細拉)

4耶和華啊,

求你使我免遭惡人的毒手,

保護我脫離殘暴之徒。

他們圖謀害我。

5傲慢人在我的路上暗設網羅,

佈下圈套,挖了陷阱。(細拉)

6耶和華啊,

我說:「你是我的上帝。」

耶和華啊,求你垂聽我的呼求。

7主耶和華,我大能的拯救者啊,

在戰爭的日子,你保護我。

8耶和華啊,

求你不要讓惡人的願望實現,

不要讓他們的陰謀得逞,

免得他們狂妄自大。(細拉)

9願那些圍攻我的人自食惡果。

10願火炭落在他們身上,

願他們被丟進火裡,

被拋進深坑,不得翻身。

11願譭謗者在地上無法立足,

願禍患毀滅殘暴之徒。

12我知道耶和華必為貧窮人伸張正義,

為困苦者伸冤。

13義人必讚美你的名,

正直人必活在你面前。