Salimo 14
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
palibe amene amachita zabwino.
2Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
amene amafunafuna Mulungu.
3Onse atembenukira kumbali,
onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
ndipo satamanda Yehova?
5Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Menneskets ondskab
1Til korlederen: En sang af David.
Tåberne mener, at Gud ikke findes.
De er fordærvede i tanke og handling.
Ingen gør det gode,
ikke én eneste.
2Fra himlen ser Herren på menneskene:
Er der nogen, der er forstandige?
Er der nogen, der søger Gud?
3Nej, alle er kommet på afveje, fordærvede af synd.
Ingen gør det gode, ikke én eneste.
4„Fatter de da intet?” siger Herren.
„De forsynder sig uden at blinke,
og de regner slet ikke med mig.”
5En dag skal de fyldes af rædsel,
for Gud er med dem, der adlyder ham.
6Onde mennesker undertrykker de svage,
men Herren er deres beskytter.
7Gid Herren ville sende sin frelse fra Zion
og redde Israels folk.
Når Herren griber ind og genrejser sit folk,
så bliver der jubel og glæde i Israel.