Masalimo 139 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 139:1-24

Salimo 139

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mwandisanthula

ndipo mukundidziwa.

2Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka;

mumazindikira maganizo anga muli kutali.

3Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga;

mumadziwa njira zanga zonse.

4Mawu asanatuluke pa lilime langa

mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.

5Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe;

mwasanjika dzanja lanu pa ine.

6Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga,

ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.

7Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu?

Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?

8Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko;

ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko.

9Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa,

ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,

10kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,

dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.

11Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu

ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”

12komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu;

usiku udzawala ngati masana,

pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.

13Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga;

munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.

14Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa;

ntchito zanu ndi zodabwitsa,

zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.

15Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu

pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi,

pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.

16Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe.

Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu

asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.

17Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu,

ndi zosawerengeka ndithu!

18Ndikanaziwerenga,

zikanakhala zochuluka kuposa mchenga;

pamene ndadzuka, ndili nanube.

19Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu!

Chokereni inu anthu owononga anzanu!

20Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa;

adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.

21Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova?

Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?

22Ndimadana nawo kwathunthu;

ndi adani anga.

23Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga;

Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.

24Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine,

ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

Ketab El Hayat

مزمور 139:1-24

الْمَزْمُورُ الْمِئَةُ وَالتَّاسِعُ وَالثَّلاثُونَ

لِقَائِدِ الْمنُشِدِينَ. مَزْمُورٌ لِدَاوُدَ

1يَا رَبُّ قَدْ فَحَصْتَنِي وَعَرَفْتَنِي. 2أَنْتَ عَرَفْتَ قُعُودِي وَقِيَامِي. فَهِمْتَ فِكْرِي مِنْ بَعِيدٍ. 3أَنْتَ تَقَصَّيْتَ مَسْلَكِي وَمَرْقَدِي، وَتَعْرِفُ كُلَّ طُرُقِي. 4عَرَفْتَ كُلَّ كَلِمَةٍ مِنْ قَبْلِ أَنْ يَتَفَوَّهَ بِها لِسَانِي. 5لَقَدْ طَوَّقْتَنِي (بِعِلْمِكَ) مِنْ خَلْفٍ وَمِنْ أَمَامٍ وَبَسَطْتَ يَدَكَ فَوْقِي. 6مَا أَعْجَبَ هَذَا الْعِلْمَ الْفَائِقَ، إِنَّهُ أَسْمَى مِنْ أَنْ أُدْرِكَهُ. 7أَيْنَ الْمَهْرَبُ مِنْ رُوحِكَ؟ أَيْنَ الْمَفَرُّ مِنْ حَضْرَتِكَ؟ 8إِنْ صَعِدْتُ إِلَى السَّمَاوَاتِ فَأَنْتَ هُنَاكَ، وَإِنْ جَعَلْتُ فِرَاشِي فِي عَالَمِ الأَمْوَاتِ فَهُنَاكَ أَنْتَ أَيْضاً. 9إِنِ اسْتَعَرْتُ أَجْنِحَةَ الْفَجْرِ وَطِرْتُ، وَسَكَنْتُ فِي أَقْصَى أَطْرَافِ الْبَحْرِ 10فَهُنَاكَ أَيْضاً يَدُكَ تَهْدِينِي وَيُمْنَاكَ تُمْسِكُنِي. 11إِنْ قُلْتُ فِي نَفْسِي: «رُبَّمَا الظُّلْمَةُ تَحْجُبُنِي وَالضَّوْءُ حَوْلِي يَصِيرُ لَيْلاً»، 12فَحَتَّى الظُّلْمَةُ لَا تُخْفِي عَنْكَ شَيْئاً، وَاللَّيْلُ كَالنَّهَارِ يُضِيءُ، فَسِيَّانَ عِنْدَكَ الظَّلامُ وَالضَّوْءُ.

13لأَنَّكَ أَنْتَ قَدْ كَوَّنْتَ كُلْيَتَيَّ. نَسَجْتَنِي دَاخِلَ بَطْنِ أُمِّي. 14أَحْمَدُكَ لأَنَّكَ صَنَعْتَنِي بِإِعْجَازِكَ الْمُدْهِشِ. مَا أَعْجَبَ أَعْمَالَكَ وَنَفْسِي تَعْلَمُ ذَلِكَ يَقِيناً. 15لَمْ يَخْفَ عَلَيْكَ كِيَانِي عِنْدَمَا كُوِّنْتُ فِي السِّرِّ، وَجُبِلْتُ فِي أَعْمَاقِ الأَرْضِ. 16رَأَتْنِي عَيْنَاكَ وَأَنَا مَازِلْتُ جَنِيناً؛ وَقَبْلَ أَنْ تُخْلَقَ أَعْضَائِي كُتِبَتْ فِي سِفْرِكَ يَوْمَ تَصَوَّرْتَهَا. 17مَا أَثْمَنَ أَفْكَارَكَ يَا اللهُ عِنْدِي! مَا أَعْظَمَ جُمْلَتَهَا! 18إِنْ أَحْصَيْتُهَا زَادَتْ عَلَى الرَّمْلِ عَدَداً. عِنْدَمَا أَسْتَيْقِظُ أَجِدُنِي مَازِلْتُ مَعَكَ. 19لَيْتَكَ يَا اللهُ تَقْتُلُ الأَشْرَارَ، فَيَبْتَعِدَ عَنِّي سَافِكُو الدِّمَاءِ. 20فَإِنَّهُمْ يَتَحَدَّثُونَ عَنْكَ بِالْمَكْرِ وَالْكَذِبِ، لأَنَّهُمْ أَعْدَاؤُكَ. 21يَا رَبُّ أَلَا أُبْغِضُ مُبْغِضِيكَ، وَأَكْرَهُ الثَّائِرِينَ عَلَيْكَ؟ 22بُغْضاً تَامّاً أُبْغِضُهُمْ، وَأَحْسِبُهُمْ أَعْدَاءَ لِي. 23تَفَحَّصْنِي يَا اللهُ وَاعْرِفْ قَلْبِي. امْتَحِنِّي وَاعْرِفْ أَفْكَارِي. 24وَانْظُرْ إنْ كَانَ فِيَّ طَرِيقُ سُوءٍ، وَاهْدِنِي الطَّرِيقَ الأَبَدِيَّ.