Masalimo 138 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 138:1-8

Salimo 138

Salimo la Davide.

1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”

2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera

ndipo ndidzayamika dzina lanu

chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,

pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu

kupambana zinthu zonse.

3Pamene ndinayitana, munandiyankha;

munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,

pamene amva mawu a pakamwa panu.

5Iwo ayimbe za njira za Yehova,

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,

koma anthu onyada amawadziwira chapatali.

7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,

mumasunga moyo wanga;

mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,

mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.

8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;

chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha

musasiye ntchito ya manja anu.

New International Version

Psalms 138:1-8

Psalm 138

Of David.

1I will praise you, Lord, with all my heart;

before the “gods” I will sing your praise.

2I will bow down toward your holy temple

and will praise your name

for your unfailing love and your faithfulness,

for you have so exalted your solemn decree

that it surpasses your fame.

3When I called, you answered me;

you greatly emboldened me.

4May all the kings of the earth praise you, Lord,

when they hear what you have decreed.

5May they sing of the ways of the Lord,

for the glory of the Lord is great.

6Though the Lord is exalted, he looks kindly on the lowly;

though lofty, he sees them from afar.

7Though I walk in the midst of trouble,

you preserve my life.

You stretch out your hand against the anger of my foes;

with your right hand you save me.

8The Lord will vindicate me;

your love, Lord, endures forever—

do not abandon the works of your hands.