Salimo 138
Salimo la Davide.
1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;
ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera
ndipo ndidzayamika dzina lanu
chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,
pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu
kupambana zinthu zonse.
3Pamene ndinayitana, munandiyankha;
munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,
pamene amva mawu a pakamwa panu.
5Iwo ayimbe za njira za Yehova,
pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,
koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,
mumasunga moyo wanga;
mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,
mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;
chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha
musasiye ntchito ya manja anu.
Psalm 138
A psalm of David.
1Lord, I will praise you with all my heart.
In front of those who think they are gods
I will sing praise to you.
2I will bow down facing your holy temple.
I will praise your name,
because you are always loving and faithful.
You have honored your holy word
even more than your own fame.
3When I called out to you, you answered me.
You made me strong and brave.
4Lord, may all the kings on earth praise you
when they hear about what you have decided.
5Lord, may they sing about what you have done,
because your glory is great.
6Though the Lord is high above all, he cares for the lowly.
Though he is in heaven above, he sees them on earth below.
7Trouble is all around me,
but you keep me alive.
You reach out your hand to put a stop to the anger of my enemies.
With your powerful right hand you save me.
8Lord, you will show that I was right to trust you.
Lord, your faithful love continues forever.
You have done so much for us, so don’t stop now.