Masalimo 138 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 138:1-8

Salimo 138

Salimo la Davide.

1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”

2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera

ndipo ndidzayamika dzina lanu

chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,

pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu

kupambana zinthu zonse.

3Pamene ndinayitana, munandiyankha;

munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,

pamene amva mawu a pakamwa panu.

5Iwo ayimbe za njira za Yehova,

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,

koma anthu onyada amawadziwira chapatali.

7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,

mumasunga moyo wanga;

mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,

mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.

8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;

chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha

musasiye ntchito ya manja anu.

Korean Living Bible

시편 138:1-8

감사의 기도

(다윗의 시)

1여호와여,

내가 진심으로

주께 감사하며

138:1 또는 ‘신들’천사들 앞에서

주를 찬양하겠습니다.

2내가 주의 성전을 향해 경배하며

주의 한결같은 사랑과

성실하심에 대하여

주의 이름을 찬양하겠습니다.

주는 그 무엇보다도

주의 이름과 말씀을 높이셨습니다.

3내가 기도할 때

주는 응답하시고

나에게 힘을 주셔서

나를 담대하게 하셨습니다.

4여호와여, 세상의 모든 왕들이

주의 말씀을 들었으니

주를 찬양할 것입니다.

5여호와의 영광이 크시므로

저들이 138:5 또는 ‘여호와의 도를’주께서 행하신 일을

노래할 것입니다.

6주는 높이 계셔도

낮은 자를 돌보시며

멀리서도 교만한 자를 아십니다.

7내가 환난을 당할지라도

주는 나를 살려내실 것이며

분노한 내 원수들을 대적하여

주의 능력으로

나를 구하실 것입니다.

8주는 138:8 또는 ‘내게 관계된 것을 완전케 하실지라’나에게 약속하신 모든 것을

이행하실 것입니다.

여호와여, 주의 사랑은 영원합니다.

주의 손으로 만든 나를

버리지 마소서.