Masalimo 138 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 138:1-8

Salimo 138

Salimo la Davide.

1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”

2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera

ndipo ndidzayamika dzina lanu

chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,

pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu

kupambana zinthu zonse.

3Pamene ndinayitana, munandiyankha;

munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,

pamene amva mawu a pakamwa panu.

5Iwo ayimbe za njira za Yehova,

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,

koma anthu onyada amawadziwira chapatali.

7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,

mumasunga moyo wanga;

mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,

mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.

8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;

chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha

musasiye ntchito ya manja anu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 138:1-8

第 138 篇

感恩的祷告

大卫的诗。

1耶和华啊,

我全心全意地称谢你,

在众神明面前歌颂你。

2我要向你的圣殿下拜,

称谢你的名,

因为你是慈爱信实的,

你显明自己的尊名和应许伟大无比。

3我祷告的时候,你就应允我;

你使我刚强壮胆。

4耶和华啊,世上所有的君王听见你的话都要称谢你。

5他们要歌唱耶和华的作为,

因为耶和华荣耀无比。

6耶和华虽在高天之上,

仍看顾卑微的人,

祂对骄傲的人也了如指掌。

7耶和华啊,虽然我身陷患难,

你必保护我的性命,

伸手攻击恼怒的仇敌,

用右手拯救我。

8耶和华必成就祂为我所定的计划;

耶和华啊,你的慈爱永远长存。

求你不要撇弃你亲手所造的。