Masalimo 137 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Thai New Contemporary Bible

สดุดี 137:1-9

สดุดี 137

1ที่ริมฝั่งแม่น้ำของบาบิโลน เรานั่งลงและร่ำไห้

เมื่อระลึกถึงศิโยน

2เราแขวนพิณของเราไว้

ที่ต้นปอปลาร์

3เพราะที่นั่น ผู้คุมขอให้เราร้องเพลง

ผู้ทรมานเราสั่งให้เราร้องเพลงแห่งความยินดี

พวกเขาพูดว่า “ไหนร้องเพลงแห่งศิโยนให้ฟังสักบทซิ!”

4เราจะขับร้องบทเพลงขององค์พระผู้เป็นเจ้า

ในดินแดนต่างด้าวได้อย่างไร?

5เยรูซาเล็มเอ๋ย หากเราลืมเจ้า

ขอให้มือขวาของเราลืมความชำนาญเถิด

6ขอให้ลิ้นของเราเกาะติดเพดานปาก

หากเราลืมเจ้า

หากเราไม่ได้ถือว่าเยรูซาเล็มเป็นสุดยอดแห่งความชื่นชมยินดี

7ข้าแต่องค์พระผู้เป็นเจ้า ขอทรงจดจำสิ่งที่ชาวเอโดมได้ทำ

ในวันที่กรุงเยรูซาเล็มแตก

พวกเขาโห่ร้องว่า “พังมันเลย”

“ทลายให้ถึงรากถึงโคนเลย!”

8โอ ธิดาแห่งบาบิโลน137:8 คือ ชาวบาบิโลนเจ้าจะพินาศย่อยยับ

ความสุขมีแก่ผู้ที่คืนสนองเจ้า

อย่างสาสมกับที่เจ้าได้ทำกับเรา

9แก่ผู้ที่จับลูกเล็กเด็กแดงของเจ้า

แล้วฟาดลงกับก้อนหิน