Masalimo 136 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 136:1-26

Salimo 136

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino.

Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

2Yamikani Mulungu wa milungu.

Pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

3Yamikani Ambuye wa ambuye,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

4Iye yekhayo amene amachita zodabwitsa zazikulu,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

5Amene mwachidziwitso chake anapanga mayiko akumwamba,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

6Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

7Amene anapanga miyuni ikuluikulu,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

8Dzuwa lilamulire usana,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

9Mwezi ndi nyenyezi zilamulire usiku,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

10Amene anakantha ana woyamba kubadwa a Igupto,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

11Natulutsa Israeli pakati pawo,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

12Ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

13Amene anagawa Nyanja Yofiira pakati,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

14Nadutsitsa Israeli pakati pa nyanjayo,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

15Koma anakokolola Farao ndi ankhondo ake mʼNyanja Yofiira,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

16Amene anatsogolera anthu ake mʼchipululu

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

17Amene anakantha mafumu akuluakulu,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

18Napha mafumu amphamvu,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

19Siloni mfumu ya Aamori,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

20Ogi mfumu ya Basani,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

21Napereka dziko lawo ngati cholowa,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

22Cholowa cha mtumiki wake Israeli;

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

23Amene anatikumbukira ife anthu opeputsidwa,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

24Amene anatimasula kwa adani athu,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

25Amene amapereka chakudya kwa cholengedwa chilichonse,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

26Yamikani Mulungu wakumwamba,

pakuti chikondi chake chosasinthika nʼchamuyaya.

Hoffnung für Alle

Psalm 136:1-26

Seine Gnade hört niemals auf!

1Dankt dem Herrn, denn er ist gut –

seine Gnade hört niemals auf!

2Dankt ihm, dem Gott über alle Götter –

seine Gnade hört niemals auf!

3Dankt ihm, dem Herrn über alle Herren –

seine Gnade hört niemals auf!

4Er allein vollbringt große Wunder –

seine Gnade hört niemals auf!

5Mit Weisheit hat er den Himmel geschaffen –

seine Gnade hört niemals auf!

6Die Erde breitete er über den Meeren aus –

seine Gnade hört niemals auf!

7Er hat die großen Lichter geschaffen –

seine Gnade hört niemals auf!

8Die Sonne, um den Tag zu bestimmen –

seine Gnade hört niemals auf!

9Mond und Sterne für die Nacht –

seine Gnade hört niemals auf!

10Alle Erstgeborenen der Ägypter tötete er –

seine Gnade hört niemals auf!

11Er führte sein Volk Israel aus Ägypten heraus –

seine Gnade hört niemals auf!

12Das alles vollbrachte er durch seine gewaltige Macht –

seine Gnade hört niemals auf!

13Er teilte das Schilfmeer –

seine Gnade hört niemals auf!

14Sein Volk ließ er mitten hindurchziehen –

seine Gnade hört niemals auf!

15Den Pharao und sein Heer aber ließ er in die Fluten stürzen –

seine Gnade hört niemals auf!

16Er führte sein Volk durch die Wüste –

seine Gnade hört niemals auf!

17Er ließ mächtige Könige umkommen –

seine Gnade hört niemals auf!

18Ja, gewaltige Herrscher tötete er –

seine Gnade hört niemals auf!

19Sihon, den König der Amoriter –

seine Gnade hört niemals auf!

20Og, den König von Baschan –

seine Gnade hört niemals auf!

21Ihre Länder übergab er Israel –

seine Gnade hört niemals auf!

22So bekam sein Volk, das ihm diente,

das ganze Gebiet als bleibenden Besitz –

seine Gnade hört niemals auf!

23Er vergaß uns nicht, als wir unterdrückt wurden –

seine Gnade hört niemals auf!

24Er befreite uns von unseren Feinden –

seine Gnade hört niemals auf!

25Allen Geschöpfen gibt er zu essen –

seine Gnade hört niemals auf!

26Ja, dankt ihm, dem Gott, der im Himmel regiert –

seine Gnade hört niemals auf!