Masalimo 135 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 135:1-21

Salimo 135

1Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;

mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

2amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,

mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;

imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,

4Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,

Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

5Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.

6Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,

kumwamba ndi dziko lapansi,

ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.

7Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,

amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula

ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

8Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.

9Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,

kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.

10Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu

ndi kupha mafumu amphamvu:

11Sihoni mfumu ya Aamori,

Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a ku Kanaani;

12ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,

cholowa cha anthu ake Aisraeli.

13Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,

mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.

14Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,

ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.

15Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,

opangidwa ndi manja a anthu.

16Pakamwa ali napo koma sayankhula

maso ali nawo, koma sapenya;

17makutu ali nawo, koma sakumva

ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.

18Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,

chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.

19Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;

inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;

20Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;

Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.

21Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,

amene amakhala mu Yerusalemu.

Tamandani Yehova.

New Russian Translation

Псалтирь 135:1-26

Псалом 135

1Славьте Господа, потому что Он благ,

потому что милость Его – навеки.

2Славьте Бога богов,

потому что милость Его – навеки.

3Славьте Владыку владык,

потому что милость Его – навеки.

4Того, Кто один творит великие чудеса,

потому что милость Его – навеки;

5премудро сотворил небеса,

потому что милость Его – навеки;

6распростер над водами землю,

потому что милость Его – навеки;

7сотворил великие светила,

потому что милость Его – навеки;

8солнце, чтобы управлять днем,

потому что милость Его – навеки;

9луну и звезды, чтобы управлять ночью,

потому что милость Его – навеки;

10Того, Кто поразил первенцев Египта135:10 См. Исх. 11 глава.,

потому что милость Его – навеки;

11вывел из его среды Израиль,

потому что милость Его – навеки,

12могучей дланью и простертой рукой,

потому что милость Его – навеки;

13Того, Кто разделил Красное море,

потому что милость Его – навеки;

14и провел сквозь него Израиль,

потому что милость Его – навеки;

15но поверг в Красное море фараона и войско его,

потому что милость Его – навеки;

16Того, Кто провел Свой народ через пустыню,

потому что милость Его – навеки;

17поразил великих царей –

потому что милость Его – навеки;

18умертвил могучих царей,

потому что милость Его – навеки;

19Сигона, царя аморреев,

потому что милость Его – навеки;

20и Ога, царя Башана135:20 См. Чис. 21:21-35.,

потому что милость Его – навеки;

21отдал их землю в наследие,

потому что милость Его – навеки;

22в наследие слуге Своему Израилю,

потому что милость Его – навеки;

23Того, Кто вспомнил нас в нашем унижении,

потому что милость Его – навеки;

24и избавил нас от врагов,

потому что милость Его – навеки;

25дает пищу всему живому,

потому что милость Его – навеки.

26Славьте Бога небес,

потому что милость Его – навеки.