Masalimo 133 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 133:1-3

Salimo 133

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu

pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!

2Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu,

otsikira ku ndevu,

ku ndevu za Aaroni,

oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.

3Zili ngati mame a ku Heremoni

otsikira pa Phiri la Ziyoni.

Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso,

ndiwo moyo wamuyaya.